< Nyimbo ya Solomoni 3 >
1 Usiku wonse ndili pa bedi langa ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda; ndinamufunafuna koma osamupeza.
Na swoim łożu wśród nocy szukałam tego, którego miłuje moja dusza. Szukałam go, ale go nie znalazłam.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda, mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake; ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda. Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
Wstanę więc już i obiegnę miasto, po ulicach i placach będę szukać tego, którego miłuje moja dusza. Szukałam go, ale nie znalazłam.
3 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzinda. “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
Znaleźli mnie strażnicy, którzy obchodzili miasto, i [spytałam]: Widzieliście tego, którego miłuje moja dusza?
4 Nditawapitirira pangʼono ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda. Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, mʼchipinda cha amene anandibereka.
A gdy ledwie od nich odeszłam, zaraz znalazłam tego, którego miłuje moja dusza. Uchwyciłam go i nie puszczę, aż go wprowadzę do domu mojej matki, do pokoju mojej rodzicielki.
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
Zaklinam was, córki Jerozolimy, na sarny i łanie polne: Nie budźcie mego umiłowanego i nie przerywajcie [jego] snu, dopóki nie zechce.
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu ngati utsi watolotolo, wonunkhira mure ndi lubani, zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
Kim jest ta, która wyłania się z pustyni jak słupy dymu, owiana wonią mirry i kadzidła oraz wszelkim wonnym proszkiem od kupca?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni, choperekezedwa ndi asilikali 60, anthu amphamvu a ku Israeli,
Oto łoże Salomona, dokoła którego [stoi] sześćdziesięciu dzielnych wojowników spośród dzielnych Izraela.
8 onse atanyamula lupanga, onse odziwa bwino nkhondo, aliyense ali ndi lupanga pambali pake, kukonzekera zoopsa za usiku.
Wszyscy trzymają miecz, wyćwiczeni w boju. Każdy z nich ma swój miecz u boku przez wzgląd na strach nocny.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi; anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
Król Salomon uczynił sobie lektykę z drzewa Libanu.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva, kumbuyo kwake kwa golide. Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo, anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi cha akazi a ku Yerusalemu.
Jej słupki uczynił ze srebra, jej pokład ze złota, podniebienie z purpury, a wnętrze wyścielone miłością córek Jerozolimy.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu, chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka pa tsiku la ukwati wake, tsiku limene mtima wake unasangalala.
Wyjdźcie, córki Syjonu, i popatrzcie na króla Salomona w koronie, którą ukoronowała go jego matka w dniu jego zaręczyn i w dniu radości jego serca.