< Nyimbo ya Solomoni 3 >

1 Usiku wonse ndili pa bedi langa ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda; ndinamufunafuna koma osamupeza.
Une nuit, étant couchée, je cherchais celui qu'aime mon âme; je le cherchais et ne le trouvais pas.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda, mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake; ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda. Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
Je veux me lever et parcourir la ville; dans les, rues et dans les places je chercherai celai qu'aime mon âme. Je le cherchai, et ne le trouvai pas.
3 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzinda. “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
Je fus rencontrée par les gardes qui parcourent la ville. « Avez-vous vu celui qu'aime mon âme? »
4 Nditawapitirira pangʼono ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda. Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, mʼchipinda cha amene anandibereka.
A peine je les avais passés, que je trouvai celui qu'aime mon âme. Je le saisis et ne le laisse point aller, que je ne l'aie conduit dans la maison de ma mère, et dans la chambre de celle qui me porta dans son sein. – –
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
Je vous adjure, filles de Jérusalem, par les gazelles ou par les biches des champs; n'éveillez pas, ne réveillez pas mon amour, plus tôt qu'elle ne voudrait!
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu ngati utsi watolotolo, wonunkhira mure ndi lubani, zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
Qui est celle qui monte ici du désert, comme des colonnes de fumée, entourée d'une vapeur de myrrhe et d'encens, et de toutes les poudres odorantes des marchands?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni, choperekezedwa ndi asilikali 60, anthu amphamvu a ku Israeli,
Voici, c'est la litière de Salomon, escortée de soixante guerriers pris parmi les guerriers d'Israël,
8 onse atanyamula lupanga, onse odziwa bwino nkhondo, aliyense ali ndi lupanga pambali pake, kukonzekera zoopsa za usiku.
tous tenant l'épée, formés au combat, ayant chacun son épée à son flanc, en vue des alarmes nocturnes.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi; anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
C'est une litière que se fit le roi Salomon, de bois du Liban.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva, kumbuyo kwake kwa golide. Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo, anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi cha akazi a ku Yerusalemu.
Il en fit les colonnes d'argent, et le dossier, d'or, le siège, de pourpre; le fond est un parquet, œuvre d'amour des filles de Jérusalem.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu, chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka pa tsiku la ukwati wake, tsiku limene mtima wake unasangalala.
Sortez et voyez, filles de Sion, le roi Salomon portant la couronne dont sa mère le couronna, au jour de ses fiançailles et au jour de la joie de son cœur.

< Nyimbo ya Solomoni 3 >