< Nyimbo ya Solomoni 3 >

1 Usiku wonse ndili pa bedi langa ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda; ndinamufunafuna koma osamupeza.
Yöllä minä vuoteellani etsin häntä, jota minun sieluni rakastaa, minä etsin, mutta en löytänyt häntä.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda, mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake; ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda. Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
"Minä nousen ja kiertelen kaupunkia, katuja ja toreja, etsin häntä, jota minun sieluni rakastaa." Minä etsin, mutta en löytänyt häntä.
3 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzinda. “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
Kohtasivat minut vartijat, jotka kaupunkia kiertävät. "Oletteko nähneet häntä, jota minun sieluni rakastaa?"
4 Nditawapitirira pangʼono ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda. Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, mʼchipinda cha amene anandibereka.
Tuskin olin kulkenut heidän ohitsensa, kun löysin hänet, jota minun sieluni rakastaa; minä tartuin häneen enkä hellittänyt hänestä, ennenkuin olin saattanut hänet äitini taloon, kantajani kammioon.
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
Minä vannotan teitä, te Jerusalemin tyttäret, gasellien tai kedon peurojen kautta: älkää herätelkö, älkää häiritkö rakkautta, ennenkuin se itse haluaa.
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu ngati utsi watolotolo, wonunkhira mure ndi lubani, zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
Mikä tuolla tulee erämaasta kuin savupatsaat, tuoksuten mirhalta ja suitsukkeelta, kaikkinaisilta kauppiaan hajujauheilta?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni, choperekezedwa ndi asilikali 60, anthu amphamvu a ku Israeli,
Katso, siinä on Salomon kantotuoli ja sen ympärillä kuusikymmentä urhoa, Israelin urhoja,
8 onse atanyamula lupanga, onse odziwa bwino nkhondo, aliyense ali ndi lupanga pambali pake, kukonzekera zoopsa za usiku.
kaikki miekkamiehiä, sotaan harjoitettuja; jokaisella on miekka kupeellansa öitten kauhuja vastaan.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi; anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
Kuningas Salomo teetti itsellensä kantotuolin Libanonin puista.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva, kumbuyo kwake kwa golide. Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo, anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi cha akazi a ku Yerusalemu.
Sen patsaat hän teetti hopeasta, sen selustan kullasta, sen istuimen purppurasta; sisältä sen koristeli Jerusalemin tyttärien rakkaus.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu, chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka pa tsiku la ukwati wake, tsiku limene mtima wake unasangalala.
Tulkaa ulos, Siionin tyttäret, ja katsokaa kuningas Salomoa, katsokaa kruunua, jolla hänen äitinsä hänet kruunasi hänen hääpäivänänsä, hänen sydämensä ilonpäivänä.

< Nyimbo ya Solomoni 3 >