< Nyimbo ya Solomoni 3 >

1 Usiku wonse ndili pa bedi langa ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda; ndinamufunafuna koma osamupeza.
At night on my bed I was longing for him whom my soul loves; I looked for him, but I could not find him.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda, mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake; ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda. Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
I said to myself, “I will get up and go through the city, through the streets and squares; I will search for him whom my soul loves.” I searched for him, but I did not find him.
3 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzinda. “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
The watchmen found me as they were making their rounds in the city. I asked them, “Have you seen him whom my soul loves?”
4 Nditawapitirira pangʼono ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda. Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, mʼchipinda cha amene anandibereka.
It was only a little while after I had passed them that I found him whom my soul loves. I held him and would not let him go until I had brought him into my mother's house, into the bedroom of the one who had conceived me.
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
I want you to swear, daughters of Jerusalem, by the gazelles and the does of the fields, that you will not awaken or arouse love until she pleases.
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu ngati utsi watolotolo, wonunkhira mure ndi lubani, zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
What is that coming up from the wilderness like a column of smoke, perfumed with myrrh and frankincense, with all the powders sold by merchants?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni, choperekezedwa ndi asilikali 60, anthu amphamvu a ku Israeli,
Look, it is the bed of Solomon; sixty warriors surround it, sixty soldiers of Israel.
8 onse atanyamula lupanga, onse odziwa bwino nkhondo, aliyense ali ndi lupanga pambali pake, kukonzekera zoopsa za usiku.
All of them are skilled with a sword and are experienced in warfare. Every man has his sword at his side, armed against the terrors of the night.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi; anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
King Solomon made himself a sedan chair of the wood from Lebanon.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva, kumbuyo kwake kwa golide. Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo, anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi cha akazi a ku Yerusalemu.
Its posts were made of silver; the back was made of gold, and the seat of purple cloth. Its interior was decorated with love by the daughters of Jerusalem.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu, chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka pa tsiku la ukwati wake, tsiku limene mtima wake unasangalala.
Go out, daughters of Zion, and gaze on King Solomon, bearing the crown with which his mother crowned him on his wedding day, on the day of the joy of his heart.

< Nyimbo ya Solomoni 3 >