< Nyimbo ya Solomoni 3 >
1 Usiku wonse ndili pa bedi langa ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda; ndinamufunafuna koma osamupeza.
All through the night [while I lay] on my bed, I longed for the one whom I love. I desired for him [to come], but he did not come.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda, mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake; ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda. Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
[So I said to myself], “I will get up now and walk around the city, through the streets and plazas, to search for the one whom I love.” [So] I [got up and] searched for him, but I could not find him.
3 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzinda. “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
The city watchmen saw me while they were patrolling/walking around the city. [I asked them], “Have you seen the one whom I love?”
4 Nditawapitirira pangʼono ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda. Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, mʼchipinda cha amene anandibereka.
As soon as I walked past them, I found the one whom I love. I clung to him and would not let him go until I had brought him to my mother’s house, to the room where my mother had conceived me (OR, where I was born).
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
You women of Jerusalem, solemnly promise me, while the does and gazelles [are listening], that you will not disturb us while we are making love until we are ready to quit.
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu ngati utsi watolotolo, wonunkhira mure ndi lubani, zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
Who is it that is coming from the desert, who is [stirring up dust] like a column of smoke from burning myrrh and incense [made from] spices [imported by] merchants?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni, choperekezedwa ndi asilikali 60, anthu amphamvu a ku Israeli,
It is [Solomon], [sitting in] his portable chair surrounded by 60 bodyguards chosen from the strongest/greatest warriors in Israel.
8 onse atanyamula lupanga, onse odziwa bwino nkhondo, aliyense ali ndi lupanga pambali pake, kukonzekera zoopsa za usiku.
They all have swords and they [all] (are trained to/know well how to) use them. Each one has his sword [strapped to] his side and [is prepared to defend Solomon from] dangers that might occur even during the night.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi; anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
King Solomon [commanded his servants] to make that portable chair for him; [it was made] with wood from Lebanon.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva, kumbuyo kwake kwa golide. Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo, anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi cha akazi a ku Yerusalemu.
The [canopy that covered it] was (held up/supported) by posts made of silver, and the back of the chair was [embroidered] with gold. The seat/cushion was covered with purple cloth lovingly made/woven by the women of Jerusalem.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu, chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka pa tsiku la ukwati wake, tsiku limene mtima wake unasangalala.
You women of Jerusalem, come and look at King Solomon wearing the headdress that his mother put on his head on the day when he was married, the day when he [SYN] was very happy.