< Nyimbo ya Solomoni 3 >

1 Usiku wonse ndili pa bedi langa ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda; ndinamufunafuna koma osamupeza.
Na ložci svém v noci hledala jsem toho, kteréhož miluje duše má. Hledala jsem ho, ale nenašla jsem ho.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda, mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake; ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda. Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
Již tedy vstanu, a zchodím město; po ryncích i po ulicech hledati budu toho, kteréhož miluje duše má. Hledala jsem ho, ale nenašla jsem ho.
3 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzinda. “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
Našli mne ponocní, kteříž chodí po městě. Viděli-liž jste toho, kteréhož miluje duše má?
4 Nditawapitirira pangʼono ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda. Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, mʼchipinda cha amene anandibereka.
A jakž jsem jich jen pominula, takž jsem našla toho, kteréhož miluje duše má. Chopila jsem ho, aniž ho pustím, až ho uvedu do domu matky své, a do pokojíka rodičky své.
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
Přísahou vás zavazuji, dcery Jeruzalémské, skrze srny a laně polní, abyste nebudily a nevyrážely ze sna milého mého, dokudž by sám nechtěl.
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu ngati utsi watolotolo, wonunkhira mure ndi lubani, zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
Která jest to, jenž vstupuje z pouště jako sloupové dymu, okouřena jsuc mirrou a kadidlem, dražším nad všelijaký prach apatekářský?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni, choperekezedwa ndi asilikali 60, anthu amphamvu a ku Israeli,
Aj, lože Šalomounovo, okolo něhož šedesáte udatných z nejsilnějších Izraelských,
8 onse atanyamula lupanga, onse odziwa bwino nkhondo, aliyense ali ndi lupanga pambali pake, kukonzekera zoopsa za usiku.
Vše vládnoucích mečem, vycvičených v boji, z nichž jeden každý má svůj meč při boku svém z příčiny strachu nočního.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi; anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
Schranu vystavěl sobě král Šalomoun z dříví Libánského,
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva, kumbuyo kwake kwa golide. Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo, anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi cha akazi a ku Yerusalemu.
Při níž udělal sloupy stříbrné, dno zlaté a ponebí šarlatové, vnitřek pak jeho postlaný milostí dcer Jeruzalémských.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu, chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka pa tsiku la ukwati wake, tsiku limene mtima wake unasangalala.
Vyjděte a pohleďte, dcery Sionské, na krále Šalomouna v koruně, kterouž ho korunovala matka jeho v den oddávání jeho a v den veselí srdce jeho.

< Nyimbo ya Solomoni 3 >