< Aroma 7 >

1 Kodi simukudziwa abale kuti Malamulo ali ndi ulamuliro pa munthu pokhapokha ngati ali ndi moyo? Ine ndikuyankhula kwa anthu amene akudziwa Malamulo.
Ta ishato tani wogaa eriza asatas yootays. Wogaa shemipora paxxa diza asa xalala harizayssa inte ereketii?
2 Mwachitsanzo, Malamulo amati mkazi wokwatiwa ndi womangidwa ndi lamulo kwa mwamuna wakeyo nthawi yonse pamene mwamuna wakeyo ali moyo. Koma ngati mwamuna wake amwalira, mkaziyo ndi womasulidwa ku lamulo la ukwati.
Issi macashi azina geliko ba azinara wogan iza qachetizay azinay paxxa diza wode gakanaskko. Azinay hayqiko iza machcho gidiza wogape anjjistaysu.
3 Koma ngati iye akwatiwa ndi mwamuna wina pamene mwamuna wake ali moyo, amatchedwa wachigololo. Koma ngati mwamuna wakeyo amwalira, mkaziyo amasuka ku lamulo ndipo si wachigololo, ngakhale kuti wakwatiwa ndi mwamuna wina.
Gido attin azinay paxxa dishin iza hara azina gelliko laymatasusu geetistaysu. Azinay hayqiko qase hara ura iza gelliko kase azina wogape anjjistadus attin layma getetuku.
4 Chimodzimodzi inunso, abale anga, munafa ku Malamulo kudzera mʼthupi la Khristu, kuti mukwatiwe ndi wina, ndi Iye amene anauka kwa akufa kuti tibalire Mulungu chipatso.
Hessa gishshi ta ishato inteka Yesus Kiristoosa asho baggara wogas hayqidista. Inte hayqope denidida kiristoosa bagga gidin nuni Xoossas ayfe ayfanaskko.
5 Pakuti pamene tinkalamulidwa ndi khalidwe lathu lauchimo, zilakolako zauchimo zimene Malamulo anaziwutsa zinkagwira ntchito mʼmatupi mwathu kotero kuti zinabala imfa.
Nagarancha medhetetha shenen nu diza wode hayqo ayfe nu ayfana mala wogay denththethida nagara amoy nu bolla oothides.
6 Koma tsopano tamasulidwa ku Malamulowo pakuti tinafa ku zimene zinkatimanga, ndipo Mzimu Woyera akutithandiza kutumikira Mulungu mʼnjira yatsopano ndipo osati mʼnjira yakale yolembedwa.
Ha7i gidiko kasse nuna waaxi qachida hayqida gishshi wogape wozetidosu. Hesikka kase cega wogan xaafetidayssan gidontta dishe ooratha ayana ogen nuni oothanaskko.
7 Nanga ife tinene chiyani? Kodi Malamulo ndi oyipa? Ayi. Nʼkosatheka! Kunena zoona, popanda Malamulo, ine sindikanazindikira tchimo. Pakuti sindikanadziwa kuti kusirira ndi tchimo ngati Malamulo sakananena kuti, “Usasirire.”
Histin nu ay ginoo? Be hu7es wogay naragaa? muleka gidena. wogaa bagara gidonttako nagaray azakone nu erokoko shin. wogay “amotofa” gonttako amoy azakone tumupe ta erikke.
8 Koma chifukwa cha Malamulo uchimo unapeza mwayi owutsa mʼkati mwanga khalidwe lililonse la kusirira. Pakuti pakanapanda Malamulo, uchimo ukanakhala wopanda mphamvu.
Nagaray qasse wogape kezida azazoy bessida ogen go7ettidi ta gidon dumma dumma iitta amo denithethides. wogay yanappe kasse nagaray hayqithiko.
9 Nthawi ina ndinali ndi moyo popanda Malamulo. Koma nditayamba kudziwa Malamulo, pomwepo uchimo unayamba kuphuka,
wogay baynida kase tani paxxa dayisse shin wogay yiini qase nagaray paxxa gidides. ta gidikko hayqadis.
10 ndipo ine ndinafa. Ine ndinazindikira kuti Malamulo omwe ankayenera kubweretsa moyo anabweretsa imfa.
He asi ashana qofetida azazoyka hayqo ekii yidaysa eradis.
11 Pakuti uchimo unapeza mwayi chifukwa cha Malamulo ndipo kudzera mʼMalamulowo, unandinyenga ndi kundiyika mu imfa.
Nagaray woga baggara bettida gaason go7ettidi tana balethidesine azazon wodhides.
12 Choncho lamulo ndi loyera, lolungama ndi labwino.
Hessa gishshi wogay ba baggara geeshshikko. azazoyka geesh, xiilone loo7okko.
13 Kodi chomwe ndi chabwino tsopano chinasanduka imfa kwa ine? Si choncho ayi! Koma kuti uchimo uzindikirike kuti ndi uchimo unabala imfa mwa ine kudzera mu chomwe chinali chabwino, kotero kuti kudzera mu lamulo uchimo ukhale oyipa kopitirira.
Gido attin loo7osu hanidaysi taas hayqos gididee? Mulekka gidena. Gido attin nagaray ba nagaratethan eretana mala loo7o gidida hano bagara ta bolla hayqo ehides. Hesikka nagaray azazo baggara kassepe aathi nagara darisides.
14 Ife tikudziwa kuti Malamulo ndi auzimu; koma ine ndine munthu wofowoka chabe, wogulitsidwa ngati kapolo ku uchimo.
Wogay ayana yo gididaysa nu erosu. Ta qasse nagaras aylle mala bayzetida asikko.
15 Ine sindizindikira zimene ndimachita. Pakuti zimene ndimafuna kuchita sindizichita koma zimene ndimadana nazo ndi zimene ndimazichita.
Tani ta oothizayssa erike. Ta oothana koyzayssa ootha erike shin ta ixxiza miishsh oothays.
16 Ndipo ngati ndimachita zimene sindimafuna kuzichita, ndiye kuti ndikuvomereza kuti lamulo ndi labwino.
Ta oothana koyontta miish oothiza gidikko wogay loo7o gididaysa ta marikatays.
17 Monga mmene zililimu, si inenso mwini amene ndimazichita zimenezi, koma tchimo limene lili mʼkati mwanga.
Hessa oothizay tana gidontta ta gaathan diza nagaray oothees.
18 Ine ndikudziwa kuti mwa ine mulibe kanthu kabwino, ndiye kuti mʼthupi langa lauchimo. Pakuti ndimafuna kuchita zabwino, koma ndimalephera kuzichita.
Tanan hesikka nagarancha gidida ta madhetetha gidon ayko loo7o miishshi baynidayssa ta erays. Loo7o oothanasi taas amotethi dees shin polla ootha erikke.
19 Ine sindichita zabwino zimene ndimafuna koma ndimachita zonyansa zimene sindikuzifuna.
Ta oothizay oothana gaada koyza loo7o ootho giden. Gido attin ta oothana koyontta iitta ootho oothays.
20 Tsopano ngati ine ndimachita zimene sindikuzifuna, si inenso amene ndimazichita, koma ndi tchimo limene lili mʼkati mwanga.
Tani oothanas koyonttayssa oothiza gidiko hessa oothizay tana gidontta ta gidon diza nagarakko.
21 Tsono ndapeza kuti lamuloli likugwira ntchito. Ngakhale ndimafuna kuchita zabwino, zoyipa zili nane pomwepo.
Hessa gishshi haysi wogay oothon dizaysi taas gellides. Hessikka tani loo7o oothana koyaysishin tani iitta oothays.
22 Mtima wanga umakondwera ndi lamulo la Mulungu.
Tani ta gaathara Xoossa wogan ufa7istays.
23 Koma mʼkati mwanga ndimaona lamulo lina likugwira ntchito kulimbana ndi zomwe mtima wanga umavomereza. Lamulo limenelo landisandutsa wamʼndende walamulo la uchimo lomwe likugwira ntchito mʼkati mwa ziwalo zanga.
Gido attin ta asatetha gidon oothiza nagara wogay tana qachi oykidi ta qofa wogara oletiza hara wogay ta asatetha gidon oothishin beyays.
24 Kalanga ine! Adzandipulumutsa ndani ku thupi la imfali?
Ta aymala laafa asee! Hayssa hayqosi imettida asatethafe tana ashanay oonee?
25 Atamandike Mulungu, amene amandipulumutsa kudzera mwa Yesu Khristu Ambuye athu! Kotero tsono, ineyo ndi mtima wanga ndimatumikira lamulo la Mulungu, koma ndi thupi langa ndimatumikira lamulo la uchimo.
Nu Goda Yesus Kiristoosa baggara galatay Xoossas gido. Histinkko tani ta baggara ta qofan Xoossa wogasi aylle gidashe tani Ta medhetetha wogan nagara wogas aylleko.

< Aroma 7 >