< Aroma 7 >
1 Kodi simukudziwa abale kuti Malamulo ali ndi ulamuliro pa munthu pokhapokha ngati ali ndi moyo? Ine ndikuyankhula kwa anthu amene akudziwa Malamulo.
Brethren, do you not know--for I am writing to people acquainted with the Law--that it is during our lifetime that we are subject to the Law?
2 Mwachitsanzo, Malamulo amati mkazi wokwatiwa ndi womangidwa ndi lamulo kwa mwamuna wakeyo nthawi yonse pamene mwamuna wakeyo ali moyo. Koma ngati mwamuna wake amwalira, mkaziyo ndi womasulidwa ku lamulo la ukwati.
A wife, for instance, whose husband is living is bound to him by the Law; but if her husband dies the law that bound her to him has now no hold over her.
3 Koma ngati iye akwatiwa ndi mwamuna wina pamene mwamuna wake ali moyo, amatchedwa wachigololo. Koma ngati mwamuna wakeyo amwalira, mkaziyo amasuka ku lamulo ndipo si wachigololo, ngakhale kuti wakwatiwa ndi mwamuna wina.
This accounts for the fact that if during her husband's life she lives with another man, she will be stigmatized as an adulteress; but that if her husband is dead she is no longer under the old prohibition, and even though she marries again, she is not an adulteress.
4 Chimodzimodzi inunso, abale anga, munafa ku Malamulo kudzera mʼthupi la Khristu, kuti mukwatiwe ndi wina, ndi Iye amene anauka kwa akufa kuti tibalire Mulungu chipatso.
So, my brethren, to you also the Law died through the incarnation of Christ, that you might be wedded to Another, namely to Him who rose from the dead in order that we might yield fruit to God.
5 Pakuti pamene tinkalamulidwa ndi khalidwe lathu lauchimo, zilakolako zauchimo zimene Malamulo anaziwutsa zinkagwira ntchito mʼmatupi mwathu kotero kuti zinabala imfa.
For whilst we were under the thraldom of our earthly natures, sinful passions-- made sinful by the Law--were always being aroused to action in our bodily faculties that they might yield fruit to death.
6 Koma tsopano tamasulidwa ku Malamulowo pakuti tinafa ku zimene zinkatimanga, ndipo Mzimu Woyera akutithandiza kutumikira Mulungu mʼnjira yatsopano ndipo osati mʼnjira yakale yolembedwa.
But seeing that we have died to that which once held us in bondage, the Law has now no hold over us, so that we render a service which, instead of being old and formal, is new and spiritual.
7 Nanga ife tinene chiyani? Kodi Malamulo ndi oyipa? Ayi. Nʼkosatheka! Kunena zoona, popanda Malamulo, ine sindikanazindikira tchimo. Pakuti sindikanadziwa kuti kusirira ndi tchimo ngati Malamulo sakananena kuti, “Usasirire.”
What follows? Is the Law itself a sinful thing? No, indeed; on the contrary, unless I had been taught by the Law, I should have known nothing of sin as sin. For instance, I should not have known what covetousness is, if the Law had not repeatedly said, "Thou shalt not covet."
8 Koma chifukwa cha Malamulo uchimo unapeza mwayi owutsa mʼkati mwanga khalidwe lililonse la kusirira. Pakuti pakanapanda Malamulo, uchimo ukanakhala wopanda mphamvu.
Sin took advantage of this, and by means of the Commandment stirred up within me every kind of coveting; for apart from Law sin would be dead.
9 Nthawi ina ndinali ndi moyo popanda Malamulo. Koma nditayamba kudziwa Malamulo, pomwepo uchimo unayamba kuphuka,
Once, apart from Law, I was alive, but when the Commandment came, sin sprang into life, and I died;
10 ndipo ine ndinafa. Ine ndinazindikira kuti Malamulo omwe ankayenera kubweretsa moyo anabweretsa imfa.
and, as it turned out, the very Commandment which was to bring me life, brought me death.
11 Pakuti uchimo unapeza mwayi chifukwa cha Malamulo ndipo kudzera mʼMalamulowo, unandinyenga ndi kundiyika mu imfa.
For sin seized the advantage, and by means of the Commandment it completely deceived me, and also put me to death.
12 Choncho lamulo ndi loyera, lolungama ndi labwino.
So that the Law itself is holy, and the Commandment is holy, just and good.
13 Kodi chomwe ndi chabwino tsopano chinasanduka imfa kwa ine? Si choncho ayi! Koma kuti uchimo uzindikirike kuti ndi uchimo unabala imfa mwa ine kudzera mu chomwe chinali chabwino, kotero kuti kudzera mu lamulo uchimo ukhale oyipa kopitirira.
Did then a thing which is good become death to me? No, indeed, but sin did; so that through its bringing about death by means of what was good, it might be seen in its true light as sin, in order that by means of the Commandment the unspeakable sinfulness of sin might be plainly shown.
14 Ife tikudziwa kuti Malamulo ndi auzimu; koma ine ndine munthu wofowoka chabe, wogulitsidwa ngati kapolo ku uchimo.
For we know that the Law is a spiritual thing; but I am unspiritual--the slave, bought and sold, of sin.
15 Ine sindizindikira zimene ndimachita. Pakuti zimene ndimafuna kuchita sindizichita koma zimene ndimadana nazo ndi zimene ndimazichita.
For what I do, I do not recognize as my own action. What I desire to do is not what I do, but what I am averse to is what I do.
16 Ndipo ngati ndimachita zimene sindimafuna kuzichita, ndiye kuti ndikuvomereza kuti lamulo ndi labwino.
But if I do that which I do not desire to do, I admit the excellence of the Law,
17 Monga mmene zililimu, si inenso mwini amene ndimazichita zimenezi, koma tchimo limene lili mʼkati mwanga.
and now it is no longer I that do these things, but the sin which has its home within me does them.
18 Ine ndikudziwa kuti mwa ine mulibe kanthu kabwino, ndiye kuti mʼthupi langa lauchimo. Pakuti ndimafuna kuchita zabwino, koma ndimalephera kuzichita.
For I know that in me, that is, in my lower self, nothing good has its home; for while the will to do right is present with me, the power to carry it out is not.
19 Ine sindichita zabwino zimene ndimafuna koma ndimachita zonyansa zimene sindikuzifuna.
For what I do is not the good thing that I desire to do; but the evil thing that I desire not to do, is what I constantly do.
20 Tsopano ngati ine ndimachita zimene sindikuzifuna, si inenso amene ndimazichita, koma ndi tchimo limene lili mʼkati mwanga.
But if I do that which I desire not to do, it can no longer be said that it is I who do it, but the sin which has its home within me does it.
21 Tsono ndapeza kuti lamuloli likugwira ntchito. Ngakhale ndimafuna kuchita zabwino, zoyipa zili nane pomwepo.
I find therefore the law of my nature to be that when I desire to do what is right, evil is lying in ambush for me.
22 Mtima wanga umakondwera ndi lamulo la Mulungu.
For in my inmost self all my sympathy is with the Law of God;
23 Koma mʼkati mwanga ndimaona lamulo lina likugwira ntchito kulimbana ndi zomwe mtima wanga umavomereza. Lamulo limenelo landisandutsa wamʼndende walamulo la uchimo lomwe likugwira ntchito mʼkati mwa ziwalo zanga.
but I discover within me a different Law at war with the Law of my understanding, and leading me captive to the Law which is everywhere at work in my body--the Law of sin.
24 Kalanga ine! Adzandipulumutsa ndani ku thupi la imfali?
(Unhappy man that I am! who will rescue me from this death-burdened body?
25 Atamandike Mulungu, amene amandipulumutsa kudzera mwa Yesu Khristu Ambuye athu! Kotero tsono, ineyo ndi mtima wanga ndimatumikira lamulo la Mulungu, koma ndi thupi langa ndimatumikira lamulo la uchimo.
Thanks be to God through Jesus Christ our Lord!) To sum up then, with my understanding, I--my true self--am in servitude to the Law of God, but with my lower nature I am in servitude to the Law of sin.