< Aroma 7 >

1 Kodi simukudziwa abale kuti Malamulo ali ndi ulamuliro pa munthu pokhapokha ngati ali ndi moyo? Ine ndikuyankhula kwa anthu amene akudziwa Malamulo.
or be ignorant brother to know for law to speak that/since: that the/this/who law to lord over the/this/who a human upon/to/against just as/how much time to live
2 Mwachitsanzo, Malamulo amati mkazi wokwatiwa ndi womangidwa ndi lamulo kwa mwamuna wakeyo nthawi yonse pamene mwamuna wakeyo ali moyo. Koma ngati mwamuna wake amwalira, mkaziyo ndi womasulidwa ku lamulo la ukwati.
the/this/who for married woman the/this/who to live man: husband to bind law if then to die the/this/who man: husband to abate away from the/this/who law the/this/who man: husband
3 Koma ngati iye akwatiwa ndi mwamuna wina pamene mwamuna wake ali moyo, amatchedwa wachigololo. Koma ngati mwamuna wakeyo amwalira, mkaziyo amasuka ku lamulo ndipo si wachigololo, ngakhale kuti wakwatiwa ndi mwamuna wina.
therefore therefore/then to live the/this/who man: husband adulterous to announce if to be man: husband other if then to die the/this/who man: husband free/freedom to be away from the/this/who law the/this/who not to exist it/s/he adulterous to be man: husband other
4 Chimodzimodzi inunso, abale anga, munafa ku Malamulo kudzera mʼthupi la Khristu, kuti mukwatiwe ndi wina, ndi Iye amene anauka kwa akufa kuti tibalire Mulungu chipatso.
so brother me and you to kill the/this/who law through/because of the/this/who body the/this/who Christ toward the/this/who to be you other the/this/who out from dead to arise in order that/to to bear fruit the/this/who God
5 Pakuti pamene tinkalamulidwa ndi khalidwe lathu lauchimo, zilakolako zauchimo zimene Malamulo anaziwutsa zinkagwira ntchito mʼmatupi mwathu kotero kuti zinabala imfa.
when for to be in/on/among the/this/who flesh the/this/who suffering the/this/who sin the/this/who through/because of the/this/who law be active in/on/among the/this/who member me toward the/this/who to bear fruit the/this/who death
6 Koma tsopano tamasulidwa ku Malamulowo pakuti tinafa ku zimene zinkatimanga, ndipo Mzimu Woyera akutithandiza kutumikira Mulungu mʼnjira yatsopano ndipo osati mʼnjira yakale yolembedwa.
now then to abate away from the/this/who law to die in/on/among which to hold back/fast so be a slave me in/on/among newness spirit/breath: spirit and no oldness something written
7 Nanga ife tinene chiyani? Kodi Malamulo ndi oyipa? Ayi. Nʼkosatheka! Kunena zoona, popanda Malamulo, ine sindikanazindikira tchimo. Pakuti sindikanadziwa kuti kusirira ndi tchimo ngati Malamulo sakananena kuti, “Usasirire.”
which? therefore/then to say the/this/who law sin not to be but the/this/who sin no to know if not through/because of law the/this/who and/both for desire no to perceive: know if not the/this/who law to say no to long for
8 Koma chifukwa cha Malamulo uchimo unapeza mwayi owutsa mʼkati mwanga khalidwe lililonse la kusirira. Pakuti pakanapanda Malamulo, uchimo ukanakhala wopanda mphamvu.
opportunity then to take the/this/who sin through/because of the/this/who commandment to workout/produce in/on/among I/we all desire without for law sin dead
9 Nthawi ina ndinali ndi moyo popanda Malamulo. Koma nditayamba kudziwa Malamulo, pomwepo uchimo unayamba kuphuka,
I/we then to live without law once/when to come/go then the/this/who commandment the/this/who sin to revive I/we then to die
10 ndipo ine ndinafa. Ine ndinazindikira kuti Malamulo omwe ankayenera kubweretsa moyo anabweretsa imfa.
and to find/meet me the/this/who commandment the/this/who toward life this/he/she/it toward death
11 Pakuti uchimo unapeza mwayi chifukwa cha Malamulo ndipo kudzera mʼMalamulowo, unandinyenga ndi kundiyika mu imfa.
the/this/who for sin opportunity to take through/because of the/this/who commandment to deceive me and through/because of it/s/he to kill
12 Choncho lamulo ndi loyera, lolungama ndi labwino.
so the/this/who on the other hand law holy and the/this/who commandment holy and just and good
13 Kodi chomwe ndi chabwino tsopano chinasanduka imfa kwa ine? Si choncho ayi! Koma kuti uchimo uzindikirike kuti ndi uchimo unabala imfa mwa ine kudzera mu chomwe chinali chabwino, kotero kuti kudzera mu lamulo uchimo ukhale oyipa kopitirira.
the/this/who therefore/then good I/we (to be *N(k)O*) death not to be but the/this/who sin in order that/to to shine/appear sin through/because of the/this/who good me to workout/produce death in order that/to to be according to surpassing sinful the/this/who sin through/because of the/this/who commandment
14 Ife tikudziwa kuti Malamulo ndi auzimu; koma ine ndine munthu wofowoka chabe, wogulitsidwa ngati kapolo ku uchimo.
to know for that/since: that the/this/who law spiritual to be I/we then (fleshly *N(k)O*) to be to sell by/under: under the/this/who sin
15 Ine sindizindikira zimene ndimachita. Pakuti zimene ndimafuna kuchita sindizichita koma zimene ndimadana nazo ndi zimene ndimazichita.
which for to workout/produce no to know no for which to will/desire this/he/she/it to do/require but which to hate this/he/she/it to do/make: do
16 Ndipo ngati ndimachita zimene sindimafuna kuzichita, ndiye kuti ndikuvomereza kuti lamulo ndi labwino.
if then which no to will/desire this/he/she/it to do/make: do to agree the/this/who law that/since: that good
17 Monga mmene zililimu, si inenso mwini amene ndimazichita zimenezi, koma tchimo limene lili mʼkati mwanga.
now then no still I/we to workout/produce it/s/he but the/this/who (to dwell *NK(o)*) in/on/among I/we sin
18 Ine ndikudziwa kuti mwa ine mulibe kanthu kabwino, ndiye kuti mʼthupi langa lauchimo. Pakuti ndimafuna kuchita zabwino, koma ndimalephera kuzichita.
to know for that/since: that no to dwell in/on/among I/we this/he/she/it to be in/on/among the/this/who flesh me good the/this/who for to will/desire be present me the/this/who then to workout/produce the/this/who good no (to find/meet *K*)
19 Ine sindichita zabwino zimene ndimafuna koma ndimachita zonyansa zimene sindikuzifuna.
no for which to will/desire to do/make: do good but which no to will/desire evil/harm: evil this/he/she/it to do/require
20 Tsopano ngati ine ndimachita zimene sindikuzifuna, si inenso amene ndimazichita, koma ndi tchimo limene lili mʼkati mwanga.
if then which no to will/desire (I/we *NK*) this/he/she/it to do/make: do no still I/we to workout/produce it/s/he but the/this/who to dwell in/on/among I/we sin
21 Tsono ndapeza kuti lamuloli likugwira ntchito. Ngakhale ndimafuna kuchita zabwino, zoyipa zili nane pomwepo.
to find/meet therefore the/this/who law the/this/who to will/desire I/we to do/make: do the/this/who good that/since: that I/we the/this/who evil/harm: evil be present
22 Mtima wanga umakondwera ndi lamulo la Mulungu.
to delight for the/this/who law the/this/who God according to the/this/who in/inner/inwardly a human
23 Koma mʼkati mwanga ndimaona lamulo lina likugwira ntchito kulimbana ndi zomwe mtima wanga umavomereza. Lamulo limenelo landisandutsa wamʼndende walamulo la uchimo lomwe likugwira ntchito mʼkati mwa ziwalo zanga.
to see then other law in/on/among the/this/who member me to wage war against the/this/who law the/this/who mind me and to capture me (in/on/among *no*) the/this/who law the/this/who sin the/this/who to be in/on/among the/this/who member me
24 Kalanga ine! Adzandipulumutsa ndani ku thupi la imfali?
wretched I/we a human which? me to rescue out from the/this/who body the/this/who death this/he/she/it
25 Atamandike Mulungu, amene amandipulumutsa kudzera mwa Yesu Khristu Ambuye athu! Kotero tsono, ineyo ndi mtima wanga ndimatumikira lamulo la Mulungu, koma ndi thupi langa ndimatumikira lamulo la uchimo.
(grace *N(K)O*) (then *no*) the/this/who God through/because of Jesus Christ the/this/who lord: God me therefore therefore/then it/s/he I/we the/this/who on the other hand mind be a slave law God the/this/who then flesh law sin

< Aroma 7 >