< Aroma 1 >

1 Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
Od Pavla, sluge Isusa Hrista, pozvanoga apostola izabranoga za jevanðelje Božije,
2 umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
Koje Bog naprijed obeæa preko proroka svojijeh u svetijem pismima
3 Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
O sinu svojemu, koji je po tijelu roðen od sjemena Davidova,
4 Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
A posvjedoèen silno za sina Božijega Duhom svetinje po vaskrseniju iz mrtvijeh, Isusu Hristu Gospodu našemu,
5 ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
Preko kojega primismo blagodat i apostolstvo, da pokorimo sve neznabošce vjeri imena njegovoga;
6 Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
Meðu kojima ste i vi pozvani Isusu Hristu,
7 Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
Svima koji su u Rimu, ljubaznima Bogu, i pozvanima svetima: blagodat vam i mir od Boga oca našega i Gospoda Isusa Hrista.
8 Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
Prvo dakle zahvaljujem Bogu svojemu kroz Isusa Hrista za sve vas što se vjera vaša glasi po svemu svijetu.
9 Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
Jer mi je svjedok Bog, kojemu služim duhom svojijem u jevanðelju sina njegova, da vas se opominjem bez prestanka,
10 Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
Moleæi se svagda Bogu u molitvama svojijem da bi mi kad Božija volja pomogla da doðem k vama;
11 Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
Jer želim vidjeti vas, da vam dam kakav duhovni dar za vaše utvrðenje,
12 ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
To jest, da se s vama utješim vjerom opštom, i vašom i mojom.
13 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
Ali vam neæu zatajiti, braæo, da sam mnogo puta htio da vam doðem, pa bih zadržan doslije, da i meðu vama imam kakav plod, kao i meðu ostalijem neznabošcima.
14 Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
Dužan sam i Grcima i divljacima, i mudrima i nerazumnima.
15 Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
Zato, od moje strane, gotov sam i vama u Rimu propovjediti jevanðelje.
16 Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
Jer se ne stidim jevanðelja Hristova; jer je sila Božija na spasenije svakome koji vjeruje, a najprije Jevrejinu i Grku.
17 Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
Jer se u njemu javlja pravda Božija iz vjere u vjeru, kao što je napisano: pravednik æe od vjere živ biti.
18 Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
Jer se otkriva gnjev Božij s neba na svaku bezbožnost i nepravdu ljudi koji drže istinu u nepravdi.
19 Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
Jer što se može doznati za Boga poznato je njima: jer im je Bog javio;
20 Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios g126)
Jer što se na njemu ne može vidjeti, od postanja svijeta moglo se poznati i vidjeti na stvorenjima, i njegova vjeèna sila i božanstvo, da nemaju izgovora. (aïdios g126)
21 Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
Jer kad poznaše Boga, ne proslaviše ga kao Boga niti mu zahvališe, nego zaludješe u svojijem mislima, i potamnje nerazumno srce njihovo.
22 Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
Kad se graðahu mudri, poludješe,
23 Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
I pretvoriše slavu vjeènoga Boga u oblièje smrtnoga èovjeka i ptica i èetvoronožnijeh životinja i gadova.
24 Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
Zato ih predade Bog u željama njihovijeh srca u neèistotu, da se pogane tjelesa njihova meðu njima samima;
25 Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
Koji pretvoriše istinu Božiju u laž, i veæma poštovaše i poslužiše tvar nego tvorca, koji je blagosloven vavijek. Amin. (aiōn g165)
26 Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
Zato ih predade Bog u sramne slasti; jer žene njihove pretvoriše putno upotrebljavanje u besputno.
27 Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
Tako i ljudi ostavivši putno upotrebljavanje ženskoga roda, raspališe se željom svojom jedan na drugoga, i ljudi s ljudima èinjahu sram, i platu koja trebaše za prijevaru njihovu primahu na sebi.
28 Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
I kao što ne marahu da poznadu Boga, zato ih Bog predade u pokvaren um da èine što ne valja,
29 Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
Da budu napunjeni svake nepravde, kurvarstva, zloæe, lakomstva, pakosti; puni zavisti, ubistva, svaðe, lukavstva, zloæudnosti;
30 osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
Šaptaèi, opadaèi, bogomrsci, siledžije, hvališe, ponositi, izmišljaèi zala, nepokorni roditeljima,
31 alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
Nerazumni, nevjere, neljubavni, neprimirljivi, nemilostivi.
32 Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.
A neki i pravdu Božiju poznavši da koji to èine zaslužuju smrt, ne samo to èine, nego pristaju na to i onima koji èine.

< Aroma 1 >