< 1 Akorinto 1 >

1 Paulo, woyitanidwa mwachifuniro cha Mulungu kuti akhale mtumwi wa Khristu Yesu ndi mʼbale wathu Sositene.
Od Pavla, voljom Božijom pozvanoga apostola Isusa Hrista, i od Sostena brata,
2 Kupita ku mpingo wa Mulungu ku Korinto, kwa oyeretsedwa mwa Khristu Yesu ndi oyitanidwa kukhala opatulika ndiponso kwa onse amene amapemphera mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu mʼdziko lonse lapansi, amene ndi Ambuye wawo ndi wathunso.
Crkvi Božijoj koja je u Korintu, osveæenima u Hristu Isusu, pozvanima svetima, sa svima koji prizivlju ime Gospoda našega Isusa Hrista na svakome mjestu i njihovome i našemu:
3 Landirani chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
Blagodat vam i mir od Boga oca našega i Gospoda Isusa Hrista.
4 Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu.
Zahvaljujem svagda Bogu svojemu za vas što vam je dana blagodat Božija u Hristu Isusu,
5 Pakuti mwa Iye mwalemekezedwa mʼnjira iliyonse, mʼkuyankhula kwanu konse ndi mʼkudziwa kwanu konse,
Te se u svemu obogatiste kroza nj, u svakoj rijeèi i svakom razumu,
6 chifukwa umboni wathu pa za Khristu unatsimikizidwa mwa inu.
Kao što se svjedoèanstvo Hristovo utvrdi meðu vama;
7 Choncho inu simusowa mphatso yauzimu iliyonse pamene mukudikira mofunitsitsa kuti Ambuye athu Yesu Khristu avumbulutsidwe.
Tako da nemate nedostatka ni u jednome daru, vi koji èekate otkrivenja Gospoda našega Isusa Hrista,
8 Adzakulimbikitsani mpaka kumapeto kuti mudzakhale wopanda mlandu pa tsiku lobwera Ambuye athu Yesu Khristu.
Koji æe vas i utvrditi do samoga kraja da budete pravi na dan Gospoda našega Isusa Hrista.
9 Mulungu amene wakuyitanani inu mu chiyanjano ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye athu ngokhulupirika.
Vjeran je Bog koji vas pozva u zajednicu sina svojega Isusa Hrista Gospoda našega.
10 Ndidandaulira inu, abale, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu kuti nonsenu muvomerezane wina ndi mnzake kuti pasakhale kugawikana pakati panu ndi kuti mukhale amodzi kwenikweni mu nzeru ndi mʼmaganizo.
Molim vas pak, braæo, imenom Gospoda našega Isusa Hrista da svi jedno govorite, i da ne budu meðu vama raspre, nego da budete utvrðeni u jednom razumu i u jednoj misli.
11 Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu.
Jer sam èuo za vas, braæo moja, od Hlojinijeh domašnjijeh da su svaðe meðu vama,
12 Chimene ndikutanthauza ndi ichi: wina amati, “Ndimatsatira Paulo,” wina, “Ndimatsatira Apolo,” wina, “Ndimatsatira Kefa,” winanso, “Ndimatsatira Khristu.”
A to kažem da jedan od vas govori: ja sam Pavlov; a drugi: ja sam Apolov; a treæi: ja sam Kifin; a èetvrti: ja sam Hristov.
13 Kodi Khristu wagawikana? Kodi Paulo anapachikidwa pa mtanda chifukwa cha inu? Kodi munabatizidwa mʼdzina la Paulo?
Eda li se Hristos razdijeli? Eda li se Pavle razape za vas? ili se u ime Pavlovo krstiste?
14 Ine ndikuyamika kuti sindinabatizepo mmodzi mwa inu kupatula Krispo ndi Gayo,
Hvala Bogu što ja nijednoga od vas ne krstih osim Krispa i Gaja;
15 mwakuti palibe amene anganene kuti anabatizidwa mʼdzina langa.
Da ne reèe ko da u svoje ime krstih.
16 (Inde, ine ndinabatizanso a mʼbanja la Stefano, koma sindikumbukira ngati ndinabatizanso wina aliyense).
A krstih i Stefanin dom: dalje ne znam jesam li koga drugog krstio.
17 Pakuti Khristu sananditume ine kudzabatiza, koma kudzalalikira Uthenga Wabwino, osati ndi mawu anzeru za umunthu, kuopa kuti mtanda wa Khristu ungakhale wopanda mphamvu.
Jer Hristos ne posla mene da krstim, nego da propovijedam jevanðelje, ne premudrijem rijeèima, da ne izgubi silu krst Hristov.
18 Pakuti uthenga wa mtanda ndi chopusa kwa iwo amene akuwonongeka, koma kwa ife amene tikupulumutsidwa uthengawu ndi mphamvu ya Mulungu.
Jer je rijeè krstova ludost onima koji ginu; a nama je koji se spasavamo sila Božija.
19 Pakuti kwalembedwa kuti, “Ine ndidzawononga nzeru za anthu anzeru; luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
Jer je pisano: pogubiæu premudrost premudrijeh, i razum razumnijeh odbaciæu.
20 Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? (aiōn g165)
Gdje je premudri? Gdje je književnik? Gdje je prepiraè ovoga vijeka? Ne pretvori li Bog mudrost ovoga svijeta u ludost? (aiōn g165)
21 Tsono poti mwa nzeru za Mulungu dziko lapansi mu nzeru zake silinamudziwe Iye, Mulungu amakondweretsedwa kuti kudzera mu chopusa cha zomwe zinalalikidwa apulumutse iwo amene akhulupirira.
Jer buduæi da u premudrosti Božijoj ne pozna svijet premudrošæu Boga, bila je Božija volja da ludošæu pouèenja spase one koji vjeruju.
22 Ayuda amafuna zizindikiro zodabwitsa ndipo Agriki amafunafuna nzeru,
Jer i Jevreji znake ištu, i Grci premudrosti traže.
23 koma ife timalalikira Khristu wopachikidwa. Chitsa chokhumudwitsa kwa Ayuda ndi chopusa kwa a mitundu ina.
A mi propovijedamo Hrista razapeta, Jevrejima dakle sablazan a Grcima bezumlje;
24 Koma kwa iwo amene Mulungu anawayitana, Ayuda ndi Agriki omwe, Khristu ndi mphamvu ya Mulungu ndi nzeru za Mulungu.
Onima pak koji su pozvani, i Jevrejima i Grcima, Hrista, Božiju silu i Božiju premudrost.
25 Pakuti za Mulungu zooneka ngati zopusa, ndi za nzeru kuposa nzeru za munthu, ndipo za Mulungu zooneka ngati zofowoka, zili ndi mphamvu kuposa mphamvu za munthu.
Jer je ludost Božija mudrija od ljudi, i slabost je Božija jaèa od ljudi.
26 Abale taganizirani mmene munalili musanayitanidwe. Si ambiri a inu munali a nzeru, si ambiri a inu munali a mphamvu zamakopedwe. Si ambiri a inu munali obadwa pa ulemerero.
Jer pogledajte znanje svoje, braæo, da nema ni mnogo premudrijeh po tijelu, ni mnogo silnijeh ni mnogo plemenitijeh;
27 Koma Mulungu anasankha zinthu zopusa za dziko lapansi kuti achititse manyazi anzeru. Mulungu anasankha zinthu zofowoka za dziko lapansi kuti achititse manyazi amphamvu.
Nego što je ludo pred svijetom ono izabra Bog da posrami premudre; i što je slabo pred svijetom ono izabra Bog da posrami jako;
28 Anasankha zinthu zapansipansi ndi zopeputsidwa za dziko la pansi lino, zinthu zimene kulibe, kuti asukulutse zimene zilipo,
I što je neplemenito pred svijetom i uništeno izabra Bog, i što nije, da uništi ono što jest,
29 kuti munthu asanyade pamaso pa Mulungu.
Da se ne pohvali nijedno tijelo pred Bogom.
30 Nʼchifukwa cha Iye kuti inu muli mwa Khristu Yesu, amene wakhala nzeru ya kwa Mulungu, kwa ife, kunena kuti kulungama kwathu, chiyero ndi chipulumutso.
Iz kojega ste vi u Hristu Isusu, koji nam posta premudrost od Boga i pravda i osveæenje i izbavljenje.
31 Choncho poti zinalembedwa kuti, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
Da kao što se piše) ko se hvali, Gospodom da se hvali.

< 1 Akorinto 1 >