< Masalimo 99 >

1 Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
יהוה מלך ירגזו עמים ישב כרובים תנוט הארץ
2 Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
יהוה בציון גדול ורם הוא על-כל-העמים
3 Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
יודו שמך גדול ונורא קדוש הוא
4 Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
ועז מלך משפט אהב אתה כוננת מישרים משפט וצדקה ביעקב אתה עשית
5 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
רוממו יהוה אלהינו והשתחוו להדם רגליו קדוש הוא
6 Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
משה ואהרן בכהניו ושמואל בקראי שמו קראים אל-יהוה והוא יענם
7 Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
בעמוד ענן ידבר אליהם שמרו עדתיו וחק נתן-למו
8 Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
יהוה אלהינו אתה עניתם אל נשא היית להם ונקם על-עלילותם
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
רוממו יהוה אלהינו והשתחוו להר קדשו כי-קדוש יהוה אלהינו

< Masalimo 99 >