< Masalimo 97 >

1 Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
INkosi iyabusa; kawuthokoze umhlaba, kazijabule izihlenge ezinengi.
2 Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
Amayezi lomnyama kuyiphahlile; ukulunga lesahlulelo kuyisisekelo sesihlalo sayo sobukhosi.
3 Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
Umlilo uhamba phambi kwayo, utshisa izitha zayo inhlangothi zonke.
4 Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
Imibane yayo ikhanyisa umhlaba; umhlaba wabona, wathuthumela.
5 Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
Izintaba zancibilika njengengcino phambi kweNkosi, phambi kweNkosi yomhlaba wonke.
6 Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
Amazulu atshumayela ukulunga kwayo, labantu bonke babona inkazimulo yayo.
7 Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
Bayayangeka bonke abakhonza izithombe, abazikhukhumeza ngezithixo; ikhonzeni, lonke bonkulunkulu.
8 Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
IZiyoni yezwa, yathokoza, lamadodakazi akoJuda athaba ngenxa yezahlulelo zakho, Nkosi.
9 Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
Ngoba wena, Nkosi, uphakeme phezu komhlaba wonke, uphakanyiswe kakhulu phezu kwabonkulunkulu bonke.
10 Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
Lina elithanda iNkosi, zondani okubi; iyagcina imiphefumulo yabangcwele bayo, ibakhulule esandleni sababi.
11 Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
Ukukhanya kuhlanyelelwe olungileyo, lentokozo abaqotho ngenhliziyo.
12 Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.
Thokozani eNkosini, lina balungileyo, libonge ekukhumbuleni ubungcwele bayo.

< Masalimo 97 >