< Masalimo 96 >

1 Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
Hlabelani eNkosini ingoma entsha; hlabelelani eNkosini, mhlaba wonke.
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Hlabelani eNkosini, lidumise ibizo layo, litshumayele usindiso lwayo insuku ngensuku.
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Landisani udumo lwayo phakathi kwezizwe, izimangaliso zayo phakathi kwabantu bonke.
4 Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
Ngoba yinkulu iNkosi, ifanele ukudunyiswa kakhulu, yona iyesabeka phezu kwabonkulunkulu bonke.
5 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
Ngoba bonke onkulunkulu bezizwe bayizithombe; kodwa iNkosi yenza amazulu.
6 Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
Ubukhosi lenkazimulo kuphambi kwayo, amandla lobuhle kusendlini yayo engcwele.
7 Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
Inikeni iNkosi, zizukulwana zezizwe, inikeni iNkosi udumo lamandla.
8 Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
Inikeni iNkosi udumo lwebizo layo; lethani umnikelo, lingene emagumeni ayo.
9 Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
Ikhonzeni iNkosi ebuhleni bobungcwele; lithuthumele phambi kwayo, mhlaba wonke.
10 Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
Tshonini phakathi kwezizwe: INkosi iyabusa. Lomhlaba umisiwe, kawuyikunyikinyeka; izabahlulela abantu ngokuqonda.
11 Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
Kawathokoze amazulu, lomhlaba ujabule; kaluhlokome ulwandle lokugcwala kwalo.
12 minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
Iganga kalithabe lakho konke okukulo. Khona izihlahla zonke zegusu zizahlabela ngentokozo
13 idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
phambi kweNkosi, ngoba iyeza, ngoba iyeza ukwahlulela umhlaba; izakwahlulela umhlaba ngokulunga, labantu ngeqiniso layo.

< Masalimo 96 >