< Masalimo 95 >
1 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
Oh pridite, zapojmo Gospodu. Naredimo radosten glas skali rešitve naše duše.
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
Pridimo pred njegovo prisotnost z zahvaljevanjem in s psalmi mu naredimo radosten zvok.
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
Kajti Gospod je velik Bog in velik Kralj nad vsemi bogovi.
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
V njegovi roki so globoki kraji zemlje; tudi moč hribov je njegova.
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
Morje je njegovo in on ga je naredil in njegove roke so oblikovale kopno zemljo.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
Oh pridite, naj obožujemo in se priklonimo; pokleknimo pred Gospodom, našim stvarnikom.
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
Kajti on je naš Bog in mi smo ljudstvo njegovega pašnika in ovce njegove roke. Če boste danes zaslišali njegov glas,
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
ne zakrknite svojega srca kakor z izzivanjem in kakor na dan preizkušnje v divjini,
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
ko so me vaši očetje skušali, me preizkušali in gledali moje delo.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
Dolgih štirideset let sem s tem rodom skupaj žaloval in rekel: »To je ljudstvo, ki se moti v svojem srcu in niso spoznali mojih poti, «
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
ki sem jim v svojem besu prisegel, da ne bodo vstopili v moj počitek.