< Masalimo 91 >

1 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
Khohni kah a huephael ah kho aka sa tah Tlungthang hlip ah rhaehrhong van ni.
2 Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
BOEIPA te, “Ka hlipyingnah neh ka rhalvong,” ka ti eh. Ka Pathen amah dongah ka pangtung eh.
3 Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
Sayuep kah pael neh talnah duektahaw khui lamkah nang te amah loh n'huul ni.
4 Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
A phaemul neh nang n'dah vaengah a phae hmuikah oltak photlinglen neh caempho khuiah na ying ni.
5 Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
Khoyin kah birhihnah khaw, khothaih kah aka thui thaltang te khaw,
6 kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
Khohmuep ah aka pongpa duektahaw khaw, khothun ah aka rhoelrhak sak lucik khaw rhih boeh.
7 Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
Na kaep ah thawngkhat, na bantang ah thawngrha cungku mai cakhaw nang taengla ha thoeih mahpawh.
8 Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
Na mik neh dawk na paelki vaengah halang rhoek kah a phainah te na hmu ni.
9 Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
Namah loh, “BOEIPA tah ka hlipyingnah koinih, “na ti tih Khohni te na khuirhung la na khueh coeng.
10 Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
Yoethae te nang taengla cuhu pawt vetih tlohtat loh na dap taengla ha moe mahpawh.
11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
Na longpuei boeih ah nang aka dawn ham a puencawn rhoek te a uen ni.
12 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
A kut neh nang n'dom uh bitni, lungto dongah na kho na khuek ve.
13 Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
Sathuengc a neh minta soah na cangdoek vetih, sathuengca neh tuihnam khaw na taelh ni.
14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
Kai taengah a ven uh dongah, anih te ka hlawt van ni. Ka ming a ming dongah, anih te ka hoeptlang ni.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
Kai n'khue vaengah anih te a taengah ka doo ni. Kai loh citcai khuiah khaw anih te ka pumcum sak vetih, amah ka thangpom ni.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”
Anih khohnin sen neh ka kodam sak vetih, kamah kah khangnah te ka hmuh sak ni.

< Masalimo 91 >