< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
BOEIPA te uem uh lah. A ming te khue uh lah. A khoboe te pilnam rhoek taengah tukkil uh lah.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Amah te hlai uh lah. Amah te tingtoeng uh lamtah amah kah khobaerhambae boeih te lolmang taeng uh lah.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
A ming cim neh thangthen uh lamtah, BOEIPA aka tlap rhoek kah a lungbuei tah a kohoe saeh.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
BOEIPA neh amah kah a sarhi te tlap lah. A maelhmai khaw tlap taitu lah.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
A kopoekrhainah a saii neh a ka dongkah laitloeknah bangla anih khobaerhambae khaw,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
A sal Abraham tiingan neh a coelh Jakob koca rhoek loh thoelh uh lah.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
BOEIPA amah ni mamih kah Pathen coeng. A laitloeknah khaw diklai pum ah om.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
A paipi tekumhal duela a thoelh dongah cadilcahma thawngkhat ham olka a uen.
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
Abraham neh Isaak taengah a saii a olhlo te,
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
Jakob taengah oltlueh la, Israel taengah kumhal paipi la a sut pah.
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
Te dongah, “Kanaan kho rhi te na rho la nang taengah kam paek ni,” na ti nah.
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
A hlang kah hlangmi te a sii la om pueng tih, a khuiah bakuep uh.
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
Te vaengah namtom taeng lamkah namtom taengla, ram pakhat lamkah pilnam pakhat taengla poengdoe uh.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Amih aka hnaemtaek ham hlang khueh pah pawt tih amih kongah manghai rhoek khaw a tluung pah.
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
Ka koelh soah ben boel lamtah ka tonghma rhoek te thaehuet thil boeh,” a ti nah.
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Khokha a khue vaengah kho khuiah conghol neh caak boeih te a phae pah.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Amih hmai kah a tueih hlang, Joseph te sal bangla a yoih.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
A kho te hlong neh a phaep pah uh a hinglu ah thicung loh a toeh.
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
A olthui a thoeng tue a pha due BOEIPA kah olthui loh ol loh anih te a cil a poe.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Manghai loh a tah dongah pilnam aka taem loh anih a doek tih a hlah.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Amah im kah boei neh a hnopai boeih aka taemrhai hamla,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
A hinglu bangla a mangpa rhoek te khoh tih a hamca rhoek te cueih sak ham te a khueh.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Te vaengah Israel loh Egypt la kun tih Jakob loh Ham kho ah bakuep.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
Tedae a pilnam te muep a pungtai sak tih a rhal rhoek lakah a yet sak.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
BOEIPA loh a sal rhoek te rhaithi sak tih, a pilnam aka hmuhuet ham Egypt rhoek kah lungbuei te a maelh pah.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
A sal Moses neh anih ham a coelh Aron te a tueih.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
Amih rhoi loh Egypt rhoek taengah Boeipa kah miknoek olka a tueng sak rhoi tih, Ham kho ah khaw kopoekrhai hno te a tueng sak rhoi.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Khohmuep a tueih tih a hmuep sak dongah Boeipa kah olthui olka te koek uh thai pawh.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
A tui te thii la a poeh sak tih a nga khaw a duek sak.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
A kho kah bukak rhoek te a manghai rhoek kah imkhui la a khae sak.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Amah loh a uen tih a khorhi tom ah pil neh pilhlip uihli tlung.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Khonal te rhael la a poeh sak tih a kho ah hmaisai hmai la coeng.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
A misur neh a thaibu te khaw a haih pah tih a khorhi kah thing te a khaem pah.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
A uen bal tih kaisih neh lungang te tae na pawt la halo.
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
Te vaengah a kho kah baelhing boeih a caak tih a khohmuen kah a thaihtae khaw a caak pah.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
A kho khuikah caming boeih neh a thahuem boeih khuikah a thaihcuek te a ngawn pah.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Te vaengah amih te cak neh, sui neh ham pawk puei dongah amah koca rhoek khuikah tah paloe pawh.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Amih Egypt rhoek te birhihnah loh a vuei tih amih rhoek a nong vaengah a kohoe uh.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Himbaiyan bangla cingmai a yaal pah tih khoyin ah hmai a vang pah.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
A bih vaengah tanghuem a khuen pah tih vaan kah buh te amih a kum sak.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Lungpang a ong vaengah tui ha phuet tih rhamrhae ah tuiva la a long sak te,
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
a sal Abraham taengkah a olkhueh cim te a poek dongah ni.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
A pilnam khaw omngaihnah tamlung a coelh neh a khuen.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
Te vaengah namtu rhoek kah a thakthaenah namtom khohmuen te a paek tih a pang uh te,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
a oltlueh ngaithuen sak ham neh a olkhueng te kueinah sak ham ni. BOEIPA te thangthen lah.

< Masalimo 105 >