< Masalimo 89 >

1 Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara. Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya; ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.
משכיל לאיתן האזרחי ב חסדי יהוה עולם אשירה לדר ודר אודיע אמונתך בפי
2 Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya, kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.
כי-אמרתי--עולם חסד יבנה שמים תכן אמונתך בהם
3 Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga, ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,
כרתי ברית לבחירי נשבעתי לדוד עבדי
4 ‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya. Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’” (Sela)
עד-עולם אכין זרעך ובניתי לדר-ודור כסאך סלה
5 Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova, kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.
ויודו שמים פלאך יהוה אף-אמונתך בקהל קדשים
6 Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova? Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?
כי מי בשחק יערך ליהוה ידמה ליהוה בבני אלים
7 Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri; Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.
אל נערץ בסוד-קדשים רבה ונורא על-כל-סביביו
8 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu? Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.
יהוה אלהי צבאות--מי-כמוך חסין יה ואמונתך סביבותיך
9 Mumalamula nyanja ya mafunde awukali; pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.
אתה מושל בגאות הים בשוא גליו אתה תשבחם
10 Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa; ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.
אתה דכאת כחלל רהב בזרוע עזך פזרת אויביך
11 Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu; munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.
לך שמים אף-לך ארץ תבל ומלאה אתה יסדתם
12 Munalenga Kumpoto ndi Kummwera; Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.
צפון וימין אתה בראתם תבור וחרמון בשמך ירננו
13 Mkono wanu ndi wamphamvu; dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.
לך זרוע עם-גבורה תעז ידך תרום ימינך
14 Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu; chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.
צדק ומשפט מכון כסאך חסד ואמת יקדמו פניך
15 Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu, amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.
אשרי העם ידעי תרועה יהוה באור-פניך יהלכון
16 Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu; amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.
בשמך יגילון כל-היום ובצדקתך ירומו
17 Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.
כי-תפארת עזמו אתה וברצונך תרים (תרום) קרנינו
18 Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova, Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.
כי ליהוה מגננו ולקדוש ישראל מלכנו
19 Kale munayankhula mʼmasomphenya, kwa anthu anu okhulupirika munati, “Ndapatsa mphamvu wankhondo; ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.
אז דברת בחזון לחסידיך-- ותאמר שויתי עזר על-גבור הרימותי בחור מעם
20 Ndamupeza mtumiki wanga Davide; ndamudzoza ndi mafuta opatulika.
מצאתי דוד עבדי בשמן קדשי משחתיו
21 Dzanja langa lidzamuchirikiza; zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.
אשר ידי תכון עמו אף-זרועי תאמצנו
22 Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho; anthu oyipa sadzamusautsa.
לא-ישיא אויב בו ובן-עולה לא יעננו
23 Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake ndi kukantha otsutsana naye.
וכתותי מפניו צריו ומשנאיו אגוף
24 Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye, ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.
ואמונתי וחסדי עמו ובשמי תרום קרנו
25 Ndidzayika dzanja lake pa nyanja, dzanja lake lamanja pa mitsinje.
ושמתי בים ידו ובנהרות ימינו
26 Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga, Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’
הוא יקראני אבי אתה אלי וצור ישועתי
27 Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa; wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.
אף-אני בכור אתנהו עליון למלכי-ארץ
28 Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya, ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.
לעולם אשמור- (אשמר-) לו חסדי ובריתי נאמנת לו
29 Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya, mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.
ושמתי לעד זרעו וכסאו כימי שמים
30 “Ngati ana ake adzataya lamulo langa ndi kusatsatira malangizo anga,
אם-יעזבו בניו תורתי ובמשפטי לא ילכון
31 ngati adzaswa malamulo anga ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,
אם-חקתי יחללו ומצותי לא ישמרו
32 Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo, mphulupulu zawo powakwapula.
ופקדתי בשבט פשעם ובנגעים עונם
33 Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye, kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.
וחסדי לא-אפיר מעמו ולא-אשקר באמונתי
34 Sindidzaswa pangano langa kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.
לא-אחלל בריתי ומוצא שפתי לא אשנה
35 Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga ndipo sindidzanama kwa Davide,
אחת נשבעתי בקדשי אם-לדוד אכזב
36 kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;
זרעו לעולם יהיה וכסאו כשמש נגדי
37 udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi, mboni yokhulupirika mʼmitambo. (Sela)
כירח יכון עולם ועד בשחק נאמן סלה
38 “Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya, mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.
ואתה זנחת ותמאס התעברת עם-משיחך
39 Mwakana pangano ndi mtumiki wanu ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.
נארתה ברית עבדך חללת לארץ נזרו
40 Inu mwagumula makoma ake onse ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.
פרצת כל-גדרתיו שמת מבצריו מחתה
41 Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake; iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.
שסהו כל-עברי דרך היה חרפה לשכניו
42 Mwakweza dzanja lamanja la adani ake; mwachititsa kuti adani ake akondwere.
הרימות ימין צריו השמחת כל-אויביו
43 Mwabunthitsa lupanga lake, simunamuthandize pa nkhondo.
אף-תשיב צור חרבו ולא הקימתו במלחמה
44 Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.
השבת מטהרו וכסאו לארץ מגרתה
45 Mwachepetsa masiku a unyamata wake; mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi. (Sela)
הקצרת ימי עלומיו העטית עליו בושה סלה
46 “Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale? Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?
עד-מה יהוה תסתר לנצח תבער כמו-אש חמתך
47 Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa pakuti munalenga kwachabe anthu onse!
זכר-אני מה-חלד על-מה-שוא בראת כל-בני-אדם
48 Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa? Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda? (Sela) (Sheol h7585)
מי גבר יחיה ולא יראה-מות ימלט נפשו מיד-שאול סלה (Sheol h7585)
49 Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija, chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?
איה חסדיך הראשנים אדני נשבעת לדוד באמונתך
50 Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera, momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,
זכר אדני חרפת עבדיך שאתי בחיקי כל-רבים עמים
51 mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova, ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.
אשר חרפו אויביך יהוה אשר חרפו עקבות משיחך
52 “Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”
ברוך יהוה לעולם אמן ואמן

< Masalimo 89 >