< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
משלי שלמה בן-דוד-- מלך ישראל
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
לדעת חכמה ומוסר להבין אמרי בינה
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
לקחת מוסר השכל צדק ומשפט ומשרים
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
לתת לפתאים ערמה לנער דעת ומזמה
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
ישמע חכם ויוסף לקח ונבון תחבלות יקנה
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
להבין משל ומליצה דברי חכמים וחידתם
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
יראת יהוה ראשית דעת חכמה ומוסר אוילים בזו
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
שמע בני מוסר אביך ואל-תטש תורת אמך
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
כי לוית חן הם לראשך וענקים לגרגרתך
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
בני-- אם-יפתוך חטאים אל-תבא
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
אם-יאמרו לכה אתנו נארבה לדם נצפנה לנקי חנם
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
נבלעם כשאול חיים ותמימים כיורדי בור (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
כל-הון יקר נמצא נמלא בתינו שלל
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
גורלך תפיל בתוכנו כיס אחד יהיה לכלנו
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
בני--אל-תלך בדרך אתם מנע רגלך מנתיבתם
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
כי רגליהם לרע ירוצו וימהרו לשפך-דם
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
כי-חנם מזרה הרשת-- בעיני כל-בעל כנף
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
והם לדמם יארבו יצפנו לנפשתם
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
כן--ארחות כל-בצע בצע את-נפש בעליו יקח
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
חכמות בחוץ תרנה ברחבות תתן קולה
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
בראש המיות תקרא בפתחי שערים בעיר--אמריה תאמר
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
עד-מתי פתים-- תאהבו-פתי ולצים--לצון חמדו להם וכסילים ישנאו-דעת
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
תשובו לתוכחתי הנה אביעה לכם רוחי אודיעה דברי אתכם
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
יען קראתי ותמאנו נטיתי ידי ואין מקשיב
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
ותפרעו כל-עצתי ותוכחתי לא אביתם
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
גם-אני באידכם אשחק אלעג בבא פחדכם
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
בבא כשאוה (כשואה) פחדכם-- ואידכם כסופה יאתה בבא עליכם צרה וצוקה
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
אז יקראנני ולא אענה ישחרנני ולא ימצאנני
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
תחת כי-שנאו דעת ויראת יהוה לא בחרו
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
לא-אבו לעצתי נאצו כל-תוכחתי
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
ויאכלו מפרי דרכם וממעצתיהם ישבעו
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
כי משובת פתים תהרגם ושלות כסילים תאבדם
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
ושמע לי ישכן-בטח ושאנן מפחד רעה

< Miyambo 1 >