< Masalimo 81 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
For the Leader; upon the Gittith. A Psalm of Asaph. Sing aloud unto God our strength; shout unto the God of Jacob.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Take up the melody, and sound the timbrel, the sweet harp with the psaltery.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Blow the horn at the new moon, at the full moon for our feast-day.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
For it is a statute for Israel, an ordinance of the God of Jacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
He appointed it in Joseph for a testimony, when He went forth against the land of Egypt. The speech of one that I knew not did I hear:
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
'I removed his shoulder from the burden; His hands were freed from the basket.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Thou didst call in trouble, and I rescued thee; I answered thee in the secret place of thunder; I proved thee at the waters of Meribah. (Selah)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Hear, O My people, and I will admonish thee: O Israel, if thou wouldest hearken unto Me!
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
There shall no strange god be in thee; neither shalt thou worship any foreign god.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
I am the LORD thy God, who brought thee up out of the land of Egypt; open thy mouth wide, and I will fill it.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
But My people hearkened not to My voice; and Israel would none of Me.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
So I let them go after the stubbornness of their heart, that they might walk in their own counsels.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
Oh that My people would hearken unto Me, that Israel would walk in My ways!
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
I would soon subdue their enemies, and turn My hand against their adversaries.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
The haters of the LORD should dwindle away before Him; and their punishment should endure for ever.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
They should also be fed with the fat of wheat; and with honey out of the rock would I satisfy thee.'