< Masalimo 66 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
For the Leader. A Song, a Psalm. Shout unto God, all the earth;
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Sing praises unto the glory of His name; make His praise glorious.
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Say unto God: 'How tremendous is Thy work! Through the greatness of Thy power shall Thine enemies dwindle away before Thee.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
All the earth shall worship Thee, and shall sing praises unto Thee; they shall sing praises to Thy name.' (Selah)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Come, and see the works of God; He is terrible in His doing toward the children of men.
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
He turned the sea into dry land; they went through the river on foot; there let us rejoice in Him!
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Who ruleth by His might for ever; His eyes keep watch upon the nations; let not the rebellious exalt themselves. (Selah)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Bless our God, ye peoples, and make the voice of His praise to be heard;
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
Who hath set our soul in life, and suffered not our foot to be moved,
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
For Thou, O God, hast tried us; Thou hast refined us, as silver is refined.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Thou didst bring us into the hold; Thou didst lay constraint upon our loins.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
Thou hast caused men to ride over our heads; we went through fire and through water; but Thou didst bring us out unto abundance.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
I will come into Thy house with burnt-offerings, I will perform unto Thee my vows,
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Which my lips have uttered, and my mouth hath spoken, when I was in distress.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
I will offer unto Thee burnt-offerings of fatlings, with the sweet smoke of rams; I will offer bullocks with goats. (Selah)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Come, and hearken, all ye that fear God, and I will declare what He hath done for my soul.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
I cried unto Him with my mouth, and He was extolled with my tongue.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
If I had regarded iniquity in my heart, the Lord would not hear;
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
But verily God hath heard; He hath attended to the voice of my prayer.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Blessed be God, who hath not turned away my prayer, nor His mercy from me.

< Masalimo 66 >