< Masalimo 75 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
A ti, oh Dios, te alabamos, a ti alabamos; y los que honran tu nombre aclaran tus obras de poder.
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
Cuando haya llegado el tiempo correcto, seré el juez en rectitud.
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
Cuando la tierra y toda su gente se debilitan, yo soy el sostén de sus pilares. (Selah)
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
Digo a los hombres de soberbia: que se haya ido tu orgullo, y a los pecadores: no se levante tu orgullo.
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
No se levante tu orgullo; no dejes más palabras de soberbia en tus cuellos estirados.
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
Porque el honor no viene del este, ni del oeste, ni del sur;
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
Pero Dios es el juez, a éste humilla y levanta a otro.
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
Porque en la mano del Señor hay una copa, y el vino es rojo; está bien mezclado, desbordando de su mano: hará que todos los pecadores de la tierra se apoderen de él, hasta la última gota.
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
Pero estaré siempre lleno de gozo, haciendo canciones de alabanza al Dios de Jacob.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
Por él cortará todos los poderíos de los pecadores; pero él poder de los rectos se levantará.