< Yobu 14 >

1 “Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
En cuanto al hombre, hijo de mujer, sus días son cortos y llenos de problemas.
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
Sale como una flor, y es cortado; sale volando como una sombra, y nunca más se ve.
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
¿Es en uno como este que tus ojos están fijos, con el propósito de juzgarlo?
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
Quién podrá sacar algo limpio de un impuro! Nadie!
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
Si sus días están ordenados, y tienes conocimiento del número de sus meses, habiéndole dado un límite fijo más allá del cual no puede ir;
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
Deja que tus ojos se aparten de él, y quita tu mano de él, para que pueda tener placer al final de su día, como un sirviente que trabaja para el pago.
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
Porque hay esperanza de un árbol; si se corta, volverá a retoñar, y sus ramas no llegarán a su fin.
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
Aunque su raíz puede ser vieja en la tierra, y su extremo cortado puede estar muerto en el polvo;
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
Aun así, con el olor del agua, hará brotes y pondrá ramas como una planta joven.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
Pero el hombre llega a su muerte y se va: abandona su espíritu, ¿y dónde está?
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
Las aguas salen de un estanque, y un río se convierte en desecho y seco;
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
Entonces el hombre baja al sepulcro y no vuelve: hasta que los cielos se acaban, no estarán despiertos ni saldrán de su sueño.
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
¡Si solo me mantuvieras a salvo en el sepulcro, poniéndome en un lugar secreto hasta que tu ira haya pasado, dándome un tiempo fijo para que pueda volver a tu memoria otra vez! (Sheol h7585)
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
Si la muerte se lleva a un hombre, ¿volverá a la vida? Todos los días de mi problema estaría esperando, hasta que llegara el momento de mi cambio.
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
Al sonido de tu voz daría una respuesta, eres aficionado a la obra de tus manos.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
Porque ahora mis pasos están numerados por ti, y mi pecado no es pasado por alto.
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
Mi maldad está sellada en una bolsa, y cosida mi iniquidad.
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
Pero verdaderamente una montaña que cae se convierte en polvo, y una roca se mueve de su lugar;
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
Las piedras son desgastadas por la fuerza de las aguas; el polvo de la tierra es arrastrado por su desbordamiento, y así pones fin a la esperanza del hombre.
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
Prevaleces sobre el siempre, y él se va; Su rostro se cambia en la muerte, y lo envías lejos.
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
Sus hijos reciben honra, y él no tiene conocimiento de ello; son humillados, pero él no es consciente de ello.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”
Ciertamente su carne sobre él tiene dolor, y su alma está lamentándose.

< Yobu 14 >