< Masalimo 75 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
“For the leader of the music. To the tune of “Do not destroy.” A psalm of Asaph.” We give thanks to thee, O God! we give thanks to thee, and near is thy name; Men shall declare thy wondrous deeds!
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
“When I see my time, Then will I judge with equity.
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
The earth trembleth, and all her inhabitants; But I uphold her pillars.”
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
I say to the proud, Behave not proudly! To the wicked, Lift not up your horn!
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
Lift not up your horn on high, And speak not with a stiff neck!
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
For promotion cometh neither from the east, nor from the west, nor from the south;
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
But it is God that judgeth; He putteth down one, and setteth up another.
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
For in the hand of the LORD there is a cup; The wine is foaming and full of spices, And of it he poureth out; Even to the dregs shall all the wicked of the earth drink it.
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
Therefore I will extol him for ever; I will sing praise to the God of Jacob.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
“I will bring down all the power of the wicked; But the righteous shall lift up their heads.”

< Masalimo 75 >