< Masalimo 66 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
(Til sangmesteren. En salme. En sang.) Bryd ud i Jubel for Gud, al Jorden,
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
lovsyng hans Navns Ære, syng ham en herlig Lovsang,
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
sig til Gud: "Hvor forfærdelige er dine Gerninger! For din vældige Styrkes Skyld logrer Fjenderne for dig,
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
al Jorden tilbeder dig, de lovsynger dig, lovsynger dit Navn." (Sela)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Kom hid og se, hvad Gud har gjort i sit Virke en Rædsel for Menneskenes Børn.
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Han forvandlede Hav til Land, de vandrede til Fods over Strømmen; lad os fryde os højlig i ham.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Han hersker med Vælde for evigt, på Folkene vogter hans Øjne, ej kan genstridige gøre sig store. (Sela)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
I Folkeslag, lov vor Gud, lad lyde hans Lovsangs Toner,
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
han, som har holdt vor Sjæl i Live og ej lod vor Fod glide ud!
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Thi du ransaged os, o Gud, rensede os, som man renser Sølv;
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
i Fængsel bragte du os, lagde Tynge på vore Lænder,
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
lod Mennesker skride hen over vort Hoved, vi kom gennem Ild og Vand; men du førte os ud og bragte os Lindring!
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Med Brændofre vil jeg gå ind i dit Hus og indfri dig mine Løfter,
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
dem, mine Læber fremførte, min Mund udtalte i Nøden.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Jeg bringer dig Ofre af Fedekvæg sammen med Vædres Offerduft, jeg ofrer Okser tillige med Bukke. (Sela)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Kom og hør og lad mig fortælle jer alle, som frygter Gud, hvad han har gjort for min Sjæl!
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Jeg råbte til ham med min Mund og priste ham med min Tunge.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
Havde jeg tænkt på ondt i mit Hjerte, da havde Herren ej hørt;
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
visselig, Gud har hørt, han lytted til min bedende Røst.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Lovet være Gud, som ikke har afvist min Bøn eller taget sin Miskundhed fra mig!

< Masalimo 66 >