< Yobu 1 >

1 Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
Der levede engang i Landet Uz en mand ved Navn Job. Det var en from og retsindig Mand, der frygtede Gud og veg fra det onde.
2 Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
Syv Sønner og tre Døtre fødtes ham;
3 ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
og hans Ejendom udgjorde 7000 Stykker Småkvæg, 3000 Kameler, 500 Spand Okser, 500 Aseninder og såre mange Trælle, så han var mægtigere end alle Østens Sønner.
4 Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
Hans Sønner havde for Skik at holde Gæstebud på Omgang hos hverandre, og de indbød deres tre Søstre til at spise og drikke sammen med sig.
5 Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
Når så Gæstebudsdagene havde nået Omgangen rundt, sendte Job Bud og lod Sønnerne hellige sig, og tidligt om Morgenen ofrede han Brændofre, et for hver af dem. Thi Job sagde: "Måske har mine Sønner syndet og forbandet Gud i deres Hjerte." Således gjorde Job hver Gang.
6 Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
Nu hændte det en Dag, at Guds Sønner kom og trådte frem for HERREN, og iblandt dem kom også Satan.
7 Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
HERREN spurgte Satan: "Hvor kommer du fra?" Satan svarede HERREN: "Jeg har gennemvanket Jorden på Kryds og tværs."
8 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
HERREN spurgte da Satan: " Har du lagt Mærke til min Tjener Job? Der findes ingen som han på Jorden, så from og retsindig en Mand, som frygter Gud og viger fra det onde."
9 Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
Men Satan svarede HERREN: "Mon det er for intet, Job frygter Gud?
10 “Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
Har du ikke omgærdet ham og hans Hus og alt, hvad han ejer, på alle Kanter? Hans Hænders Idræt har du velsignet, og hans Hjorde breder sig i Landet.
11 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Men ræk engang din Hånd ud og rør ved alt, hvad han ejer! Sandelig, han vil forbande dig lige op i dit Ansigt!"
12 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
Da sagde HERREN til Satan: "Se, alt hvad han ejer, er i din Hånd; kun mod ham selv må du ikke udrække din Hånd!" Så gik Satan bort fra HERRENs Åsyn.
13 Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
Da nu en Dag hans Sønner og Døtre spiste og drak i den ældste Broders Hus,
14 wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
kom et Sendebud til Job og sagde: "Okserne gik for Ploven, og Aseninderne græssede i Nærheden;
15 tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
så faldt Sabæerne over dem og tog dem; Karlene huggede de ned med Sværdet; jeg alene undslap for at melde dig det."
16 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Medens han endnu talte, kom en anden og sagde: "Guds Ild faldt ned fra Himmelen og slog ned iblandt Småkvæget og Karlene og fortærede dem; jeg alene undslap for at melde dig det."
17 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Medens han endnu talte, kom en tredje og sagde: "Kaldæerne kom i tre Flokke og kastede sig over Kamelerne og tog dem; Karlene huggede de ned med Sværdet; jeg alene undslap for at melde dig det."
18 Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
Medens han endnu talte, kom en fjerde og sagde: "Dine Sønner og Døtre spiste og drak i deres ældste Broders Hus;
19 mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
og se, da for der et stærkt Vejr hen over Ørkenen, og det tog i Husets fire Hjørner, så det styrtede ned over de unge Mænd, og de omkom; jeg alene undslap for at melde dig det."
20 Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
Da stod Job op, sønderrev sin Kappe, skar sit Hovedhår af og kastede sig til Jorden, tilbad
21 nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
og sagde: Nøgen kom jeg af Moders Skød, og nøgen vender jeg did tilbage. HERREN gav, og HERREN tog, HERRENs Navn være lovet!"
22 Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”
I alt dette syndede Job ikke og tillagde ikke Gud noget vrangt.

< Yobu 1 >