< Masalimo 60 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
För sångmästaren, efter »Vittnesbördets lilja»; en sång, till att inläras; av David,
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
när han var i fejd med Aram-Naharaim och Aram-Soba, och Joab kom tillbaka och slog edoméerna i Saltdalen, tolv tusen man.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
Gud, du har förkastat och förskingrat oss, du har varit vred; upprätta oss igen.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
Du har kommit jorden att bäva och rämna; hela nu dess revor, ty den vacklar.
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Du har låtit ditt folk se hårda ting, du har iskänkt åt oss rusande vin.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
Men åt dem som frukta dig gav du ett baner, dit de kunde samla sig för att undfly bågen. (Sela)
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
På det att dina vänner må varda räddade, må du giva seger med din högra hand och bönhöra oss.
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
Gud har talat i sin helgedom: »Jag skall triumfera, jag skall utskifta Sikem och skall avmäta Suckots dal.
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Mitt är Gilead, och mitt är Manasse, Efraim är mitt huvuds värn, Juda min härskarstav;
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
Moab är mitt tvagningskärl, på Edom kastar jag min sko; höj jubelrop till min ära, du filistéernas land.»
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
Vem skall föra mig till den fasta staden, vem leder mig till Edom?
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.
Har icke du, o Gud, förkastat oss, så att du ej drager ut med våra härar, o Gud? Giv oss hjälp mot ovännen; ty människors hjälp är fåfänglighet. Med Gud kunna vi göra mäktiga ting; han skall förtrampa våra ovänner.