< Masalimo 60 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
Kumqondisi wokuhlabelela. Kulandelwa itshuni ethi, “Iluba lesiVumelwano.” Imikithamu kaDavida. Elokufundisa. Lapho alwa lo-Aramu Naharayimu lo-Aramu Zobha, njalo lapho uJowabi athi ekubuyeni kwakhe walahla phansi ama-Edomi azinkulungwane ezilitshumi lambili eSigodini seTswayi. Ususilahlile, Oh Nkulunkulu, wabhidliza izinqaba zethu; ubukade uthukuthele, manje ake usivuselele!
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
Usulizamazamisile ilizwe waliqhekeza; namathisela iminkenke yalo ngoba selivevezela.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
Ubabonisile abantu bakho izikhathi ezilukhuni; usiphe iwayini elisenza sidiyazele.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
Kodwa kulabo abakwesabayo usuphakamise uphawu lokubahlanganisa ndawonye.
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Sisindise, usisize ngesandla sakho sokunene, ukuze bonke labo obathandayo bakhululwe.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
UNkulunkulu usekhulumile esendlini yakhe engcwele: “Ngokunqoba ngizayaba iShekhemu, ngihlole leSigodi saseSukhothi.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
Ngeyami iGiliyadi, loManase ngowami; u-Efrayimi yisivikelo sekhanda lami, uJuda uyintonga yami yobukhosi.
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
IMowabi ngumganu wami wokugezela, phezu kuka-Edomi ngiphosela amanyathelo ami; phezu kweFilistiya ngihalalisa umkhosi wokunqoba.”
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Ngubani ozangisa emzini olenqaba na? Ngubani ozangiholela e-Edomi na?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
Kakusuwe na, Oh Nkulunkulu, wena osusilahlile, ongasaphumi lathi ezimpini zethu?
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
Ake usisize ezitheni zethu, ngoba usizo lomuntu luyize.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.
Nxa siloNkulunkulu sizanqoba, njalo uzazinyathelela phansi izitha zethu.