< Masalimo 60 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
[I prayed], “God, you have rejected us [Israelis]! Because you have been angry [with us], you have [enabled our enemies] to break through our ranks. [Please] enable us to be strong again!
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
[When we were defeated, it was as though] [MET] there was a big earthquake in our land that caused the ground to split open. So now, [just as only you can] cause the cracks in the land to disappear, [help our army to be strong again], because [it is as though] our country is (falling apart/being destroyed).
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
You have caused [us], your people, to suffer very much; [it is as though] you forced us to drink [strong] wine that caused us to stagger around [after we became drunk].
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
But you have raised a battle flag for those who revere you in order that they can gather around it and not [be killed by the enemies’] arrows.
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Answer our [prayers] and enable us by your power [MTY] to defeat [our enemies] in order that we, the people whom you love, will be saved.”
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
[Then] God [answered my prayer and] spoke from his temple, saying, “Because I have conquered [your enemies], I will divide up [everything in] Shechem [city], and I will distribute it among my people [the land in] Succoth Valley.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
The Gilead [region] is mine; the [people of the tribe of] Manasseh are mine; [the tribe of] Ephraim is [like] my helmet [MET]; and [the tribe of] Judah is [like] the (scepter/stick [that I hold which shows that I am the ruler]) [MET];
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
but the Moab [region] is [like] my washbasin [MET]; I throw my sandal in the Edom [area to show that it belongs to me]; I shout triumphantly because I have defeated [the people of] the Philistia [area].”
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
[Because I want to defeat the people of] Edom, (who will lead my [army triumphantly] to their [capital] city that has strong walls around it?/I want someone to lead my [army triumphantly] to their [capital] city that has strong walls around it.)” [RHQ]
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
So, God, we [desire/hope that] [RHQ] you have not truly abandoned us, and that you will go with us when our armies march out [to fight our enemies].
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
[We need you to] help us when we fight against our enemies, because the help that humans can give us is worthless.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.
But with you [helping us], we shall win; you will enable us to defeat our enemies.