< Masalimo 60 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
God, you have rejected us. You have broken us down. You have been angry. Restore us, again.
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
You have made the land tremble. You have torn it. Mend its fractures, for it quakes.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
You have shown your people hard things. You have made us drink the wine that makes us stagger.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
You have given a banner to those who fear you, that it may be displayed because of the truth. (Selah) ·contemplation with musical interlude·.
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
So that your yadid ·beloved· may be delivered, save with your right hand, and answer us.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
God has spoken from his sanctuary: “I will triumph. I will divide Shechem, and measure out the valley of Sukkot.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
Gilead is mine, and Manasseh [Causing to forget] is mine. Ephraim [Fruit] also is the defense of my head. Judah [Praised] is my scepter.
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
Moab [From father] is my wash basin. I will throw my shoe on Edom [Red]. I shout in triumph over Philistia.”
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Who will bring me into the strong city? Who has led me to Edom [Red]?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
Haven’t you, God, rejected us? You don’t go out with our armies, God.
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
Give us help against the adversary, for the help of man is vain.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.
Through God we shall do valiantly, for it is he who will tread down our adversaries.

< Masalimo 60 >