< Masalimo 60 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
Unto the end, for them that shall be changed, for the inscription of a title, to David himself, for doctrine, When he set fire to Mesopotamia of Syria and Sobal and Joab returned and slew of Edom, in the vale of the saltpits, twelve thousand men. O God, thou hast cast us off, and hast destroyed us; thou hast been angry, and hast had mercy on us.
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
Thou hast moved the earth, and hast troubled it: heal thou the breaches thereof, for it has been moved.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
Thou hast shewn thy people hard things; thou hast made us drink wine of sorrow.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
Thou hast given a warning to them that fear thee: that they may flee from before the bow: That thy beloved may be delivered.
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Save me with thy right hand, and hear me.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
God hath spoken in his holy place: I will rejoice, and I will divide Sichem; and will mete out the vale of tabernacles.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
Galaad is mine, and Manasses is mine: and Ephraim is the strength of my head. Juda is my king:
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
Moab is the pot of my hope. Into Edom will I stretch out my shoe: to me the foreigners are made subject.
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Who will bring me into the strong city? who will lead me into Edom?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
Wilt not thou, O God, who hast cast us off? and wilt not thou, O God, go out with our armies?
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
Give us help from trouble: for vain is the salvation of man.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.
Through God we shall do mightily: and he shall bring to nothing them that afflict us.

< Masalimo 60 >