< Masalimo 60 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
For the end, for them that shall yet be changed; for an inscription by David for instruction, when he [had] burnt Mesopotamia of Syria, and Syria Sobal, and Joab [had] returned and struck [in] the valley of salt twelve thousand. O God, you have rejected and destroyed us; you have been angry, yet have pitied us.
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
You have shaken the earth, and troubled it; heal its breaches, for it has been shaken.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
You have shown your people hard things: you has made us drink the wine of astonishment.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
You have given a token to them that fear you, that they might flee from the bow. (Pause)
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
That your beloved ones may be delivered; save with your right hand, and hear me.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
God has spoken in his holiness; I will rejoice, and divide Sicima, and measure out the valley of tents.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
Galaad is mine, and Manasse is mine; and Ephraim is the strength of my head;
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
Judas is my king; Moab is the cauldron of my hope; over Idumea will I stretch out my shoe; the Philistines have been subjected to me.
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Who will lead me into the fortified city? who will guide me as far a Idumea?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
Will not you, O God, who have cast us off? and will not you, O God, go forth with our forces?
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
Give us help from trouble: for vain is the deliverance of man.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.
In God will we do valiantly; and he shall bring to nothing them that harass us.

< Masalimo 60 >