< Masalimo 60 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
達味金詩,交與樂官。 約阿布歸來,在鹽谷殺了一萬二千人。 天主,你拋棄了我們,粉碎了我們!你曾發怒,今求你復興我們。
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
你曾使大地震動,使地裂土崩,求你彌補裂縫,因它搖搖不定。
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
你使你的百姓遭受艱苦,使我們喝了麻醉的烈酒。
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
然後你為敬愛你的人,豎起旗幟,為使他們閃避仇敵的弓矢;
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
為叫你所愛的人,獲得救恩;求你以右手協助,垂允我們。
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
天主在自己的聖所說:「我要凱旋,將舍根分疆,將穌苛特的平原測量。
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
基肋阿得地屬於我,默納協地也屬於我;我的頭盔就是厄弗辣因,猶大成為我手中的權棍;
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
摩阿布是我的沐浴池,我向厄東投我的鞋隻,我還要戰勝培肋舍特。
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
誰弔領我進入堅城,誰領導我走進厄東?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
天主,莫非你已將我們拋棄,難道不率領我軍出擊?
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
求你援助我們抵抗仇讎,因為人的援助盡是虛無。
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.
我們倚靠天主奮勇行事,祂必要,踐踏我們的仇敵。

< Masalimo 60 >