< Masalimo 60 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
O Yuus, jago yumutejam, jago gumapotjam papa; guinin lalalojao; O, natalojam guato.
2 Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
Jago jagasja munamayengyong y tano; jago yumulang; nafanjomlo y yinilangña sija, sa manmayeyengyong.
3 Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
Unfanue y taotaomo sija ni y manmajetog na güinaja; unnafanguimenjam ni y binon na matulalaejon.
4 Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
Unnae ayo sija ni y manmaañao nu jago, un bandera para ujatsa pot y minagajet. (Sila)
5 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Sa para ufanlibre y güinaeyamo; satba ni y agapa na canaemo, yan opejam.
6 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
Si Yuus sumangan y sinantosña; siempre jumagof; ya siempre judibide iya Siquem, ya jumide y bayen Sucot.
7 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
Iyoco Galaad, ya iyoco Manases: Efraim y guinegüe y ilujo; Juda y baston minagasso.
8 Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
Moab, y palanggana para jufagagaseyo; y jilo Edom nae juyute y sapatosso: Filistia, agangjao pot guajo.
9 Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Jaye uchinileyo guato gui fitme na siuda? jaye uesgaejonyo guato Edom?
10 Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
Mungajao, O Yuus, ni y guinin yumutejam? yan jago, O Yuus, ti jumanao yan y inetnon sendalonmame.
11 Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
Naejam inayuda contra y contrario gui chinatsaga; sa taebale y inayudan taotao.
12 Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.
Guinin as Yuus nae infatinas y minatatnga; sa güiyaja ni ugacha papa y contrarionmame.

< Masalimo 60 >