< Masalimo 59 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
For the Leader; Al-tashheth. A Psalm of David; Michtam; when Saul sent, and they watched the house to kill him. Deliver me from mine enemies, O my God; set me on high from them that rise up against me.
2 Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
Deliver me from the workers of iniquity, and save me from the men of blood.
3 Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
For, lo, they lie in wait for my soul; the impudent gather themselves together against me; not for my transgression, nor for my sin, O LORD.
4 Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
Without my fault, they run and prepare themselves; awake Thou to help me, and behold.
5 Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
Thou therefore, O LORD God of hosts, the God of Israel, arouse Thyself to punish all the nations; show no mercy to any iniquitous traitors. (Selah)
6 Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
They return at evening, they howl like a dog, and go round about the city.
7 Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
Behold, they belch out with their mouth; swords are in their lips: 'For who doth hear?'
8 Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
But Thou, O LORD, shalt laugh at them; Thou shalt have all the nations in derision.
9 Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
Because of his strength, I will wait for Thee; for God is my high tower.
10 Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
The God of my mercy will come to meet me; God will let me gaze upon mine adversaries.
11 Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
Slay them not, lest my people forget, make them wander to and fro by Thy power, and bring them down, O Lord our shield.
12 Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
For the sin of their mouth, and the words of their lips, let them even be taken in their pride, and for cursing and lying which they speak.
13 muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
Consume them in wrath, consume them, that they be no more; and let them know that God ruleth in Jacob, unto the ends of the earth. (Selah)
14 Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
And they return at evening, they howl like a dog, and go round about the city;
15 Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
They wander up and down to devour, and tarry all night if they have not their fill.
16 Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
But as for me, I will sing of Thy strength; yea, I will sing aloud of Thy mercy in the morning; for Thou hast been my high tower, and a refuge in the day of my distress.
17 Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.
O my strength, unto Thee will I sing praises; for God is my high tower, the God of my mercy.