< Masalimo 57 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
Til Sangmesteren; „fordærv ikke”; af David; „et gyldent Smykke”; der han flyede fra Sauls Ansigt i Hulen.
2 Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
Gud! vær mig naadig, vær mig naadig; thi min Sjæl forlader sig paa dig, og under dine Vingers Skygge søger jeg Ly, indtil al Ulykken er gaaet over.
3 Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
Jeg vil raabe til Gud, den Højeste, til den Gud, som udfører min Sag.
4 Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
Han skal sende fra Himmelen og frelse mig; den, som vilde opsluge mig, haaner. (Sela) Gud skal sende sin Miskundhed og sin Sandhed.
5 Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Min Sjæl er iblandt Løver, jeg maa ligge imellem dem, som sprude Ild, Menneskens Børn, hvis Tænder ere Spyd og Pile, og hvis Tunge er et skarpt Sværd.
6 Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
Gud! ophøj dig over Himlene, din Ære være over al Jorden!
7 Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
De stillede Garn for mine Trin, min Sjæl nedbøjede sig; de grove en Grav for mit Ansigt, de faldt selv midt i den. (Sela)
8 Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
Gud! mit Hjerte er trøstigt, mit Hjerte er trøstigt; jeg vil synge og lege paa Harpe.
9 Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
Vaagn op, min Ære! vaagn op, Psalter og Harpe! jeg vil vække Morgenrøden.
10 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
Herre! jeg vil takke dig iblandt Folkene; jeg vil lege paa Harpe for dig iblandt Folkestammer.
11 Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
Thi din Miskundhed er stor indtil Himlene og din Sandhed indtil Skyerne. Gud! ophøj dig over Himlene, din Ære være over al Jorden.