< Masalimo 46 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali. Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.
UNkulunkulu uyisiphephelo sethu lamandla ethu, uyatholwa elusizo kakhulu ekuhluphekeni.
2 Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike, ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,
Ngenxa yalokhu kasiyikwesaba ekuguqukeni komhlaba, lanxa izintaba zidilikela phakathi kwenlwandle.
3 ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu, ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.
Amanzi alo kawahlokome, akhaphazele, izintaba zizamazame ngokukhukhumala kwalo. (Sela)
4 Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu, malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.
Kulomfula, izifula zawo zithokozisa umuzi kaNkulunkulu, indawo engcwele yamathabhanekele oPhezukonke.
5 Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa; Mulungu adzawuthandiza mmawa.
UNkulunkulu uphakathi kwawo, kawuyikunyikinywa; uNkulunkulu uzawusiza ngovivi lokusa.
6 Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa; Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.
Izizwe ziyaxokozela, imibuso izamazame; wakhupha ilizwi lakhe, umhlaba wancibilika.
7 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
INkosi yamabandla ilathi, uNkulunkulu kaJakobe uyinqaba yethu. (Sela)
8 Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova, chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.
Wozani libone imisebenzi yeNkosi, incithakalo eyenzileyo emhlabeni.
9 Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi; Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo; amatentha zishango ndi moto.
Yenza izimpi ziphele kuze kube semkhawulweni womhlaba; yephula idandili, iqumaqume umkhonto, itshise izinqola emlilweni.
10 Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu; ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu; ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”
Thulani, lazi ukuthi mina nginguNkulunkulu, ngizaphakanyiswa phakathi kwezizwe, ngiphakanyiswe emhlabeni.
11 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
INkosi yamabandla ilathi, uNkulunkulu kaJakobe uyinqaba yethu. (Sela)

< Masalimo 46 >