< Masalimo 45 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
Inhliziyo yami iphuphuma ngendaba enhle; ngikhuluma ngezinto engizenzele inkosi; ulimi lwami lulusiba lombhali ophangisayo.
2 Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
Umuhle kulabantwana babantu; umusa uthululwe endebeni zakho; ngenxa yalokho uNkulunkulu ukubusisile kuze kube phakade.
3 Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
Bhinca inkemba yakho emlenzeni, qhawe, udumo lwakho lobukhosi bakho.
4 Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
Lebukhosini bakho gada uphumulele, ngenxa yeqiniso lobumnene bokulunga; lesandla sakho sokunene sikufundise izinto ezesabekayo.
5 Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
Imitshoko yakho ibukhali enhliziyweni yezitha zenkosi; izizwe zizakuwa ngaphansi kwakho.
6 Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
Isihlalo sakho sobukhosi, Nkulunkulu, ngesaphakade laphakade; intonga yakho yobukhosi iyintonga yobuqotho.
7 Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
Uthanda ukulunga, njalo uzonda ububi; ngenxa yalokho uNkulunkulu, uNkulunkulu wakho, ukugcobile ngamafutha entokozo ngaphezu kwabanakwenu.
8 Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
Izembatho zakho zonke ziqholiwe ngemure lenhlaba lekhasiya; ezigodlweni zempondo zendlovu abakwenze wathokoza ngazo.
9 Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
Amadodakazi amakhosi aphakathi kwabesifazana bakho abadumileyo; indlovukazi imi esandleni sokunene sakho yembethe igolide leOfiri.
10 Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
Zwana, ndodakazi, unakane, ubeke indlebe yakho; ukhohlwe abantu bakini lendlu kayihlo;
11 Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
khona inkosi izalangatha ubuhle bakho; ngoba iyinkosi yakho, njalo khothama kuyo.
12 Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
Lendodakazi yeTire ilesipho, labanothileyo ebantwini, bazancenga ubuso bakho.
13 Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
Indodakazi yenkosi iyakhazimula yonke ngaphakathi, isembatho sayo singesegolide elelukiweyo.
14 Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
Izalethwa enkosini yembethe isembatho esifekethisiweyo; izintombi eziyilandelayo, abangane bayo, zizalethwa kuwe.
15 Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
Zizalethwa ngokuthaba lenjabulo, zizangena esigodlweni senkosi.
16 Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
Esikhundleni saboyihlo kuzakuba ngamadodana akho, uzawabeka abe yiziphathamandla emhlabeni wonke.
17 Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.
Ibizo lakho ngizalenza likhunjulwe ezizukulwaneni zonke; ngenxa yalokho izizwe zizakudumisa kuze kube nini lanini.

< Masalimo 45 >