< Masalimo 44 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
Au chef des chantres. Par les fils de Coré. Maskîl. O Dieu! De nos oreilles nous l’avons entendue, nos pères nous l’ont racontée, l’œuvre que tu as accomplie de leurs jours, aux temps antiques.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Toi, de ta main, tu as dépossédé des nations, et tu les as implantés, eux; tu as ruiné des peuplades, et eux, tu les as multipliés.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
Certes, ce n’est pas leur épée qui les a faits maîtres du pays, ni leur bras qui leur a donné la victoire: c’est ta droite, ton bras, la lumière de ta face; car tu les avais pris en affection.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
C’Est toi qui es mon roi, ô Dieu! Décrète les triomphes de Jacob.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Grâce à toi nous enfonçons nos ennemis, avec l’aide de ton nom, nous écrasons nos agresseurs.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
Car je ne mets pas ma confiance en mon arc; ce n’est pas mon épée qui m’assure la victoire;
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
mais c’est toi qui nous fait triompher de nos ennemis, qui couvres de confusion ceux qui nous haïssent.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
En Dieu nous nous glorifions sans cesse, et à jamais nous célébrons ton nom. (Sélah)
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
Pourtant tu nous as rejetés et humiliés, et tu n’accompagnes plus nos armées.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
Tu nous fais reculer devant l’ennemi: ceux qui nous haïssent pillent à leur aise.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
Tu nous livres comme des troupeaux dont on se nourrit, et nous éparpilles parmi les nations.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
Tu vends ton peuple à vil prix; tu n’estimes pas bien haut sa valeur.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
Tu fais de nous un objet d’opprobre pour nos voisins, la risée et la moquerie de notre entourage.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
Tu nous rends la fable des nations; nous excitons des hochements de tête parmi les peuples.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
Tout le temps, mon déshonneur est là, sous mes yeux, et mon visage se couvre de honte
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
à la voix de l’insulteur et du détracteur, à la vue de l’ennemi, avide de vengeance.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
Tout cela nous est advenu, sans que nous t’ayons oublié, sans que nous ayons trahi ton alliance.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
Notre cœur n’a pas rétrogradé, ni nos pas n’ont dévié de ton chemin,
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
pour que tu dusses nous reléguer dans la région des monstres et nous recouvrir des ombres de la mort.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
Si nous avions oublié le nom de notre Dieu, étendu les mains vers un dieu étranger,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
est-ce que Dieu ne l’aurait pas constaté, puisqu’il connaît les secrets du cœur?
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
Mais pour toi nous subissons chaque jour la mort; on nous considère comme des brebis destinées à la boucherie.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Réveille-toi donc! Pourquoi demeures-tu endormi, Seigneur? Sors de ton sommeil, ne nous délaisse pas à jamais.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Pourquoi dérobes-tu ta face, oublies-tu notre misère et notre oppression?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
Car notre âme est abaissée jusque dans la poussière, notre corps est couché de son long sur le sol.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Lève-toi pour nous venir en aide, délivre-nous par un effet de ta bonté!

< Masalimo 44 >