< Yobu 1 >

1 Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
II y avait dans le pays d’Ouç un homme du nom de Job; cet homme était intègre et droit, craignant Dieu et évitant le mal.
2 Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
Il lui était né sept fils et trois filles.
3 ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
Il possédait sept mille brebis, trois mille chameaux, cinq cents paires de bœufs, cinq cents ânesses et de très nombreux gens de service. Et cet homme était le plus considérable de tous les habitants de l’Orient.
4 Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
Ses fils avaient coutume d’organiser un festin dans la maison de chacun d’eux à tour de rôle; ils faisaient aussi convier leurs trois sœurs à manger et à boire avec eux.
5 Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
Et lorsque le cycle de ces jours de festin était révolu, Job envoyait chercher ses fils pour les purifier; il se levait de grand matin et offrait un holocauste pour chacun d’eux, car Job se disait: "Peut-être mes enfants auront-ils commis quelque péché et renié Dieu en leur cœur." C’Est ainsi qu’agissait Job en tout temps.
6 Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
Or, un jour les fils de Dieu vinrent se présenter devant l’Eternel, et le Satan, lui aussi, vint au milieu d’eux.
7 Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
L’Eternel dit au Satan: "D’Où viens-tu?" Le Satan répondit au Seigneur et dit: "J’Ai visité la terre 'et l’ai parcourue en tous sens."
8 Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
L’Eternel demanda au Satan: "As-tu porté ton attention sur mon serviteur Job? Certes, il n’a point son pareil sur la terre, tellement il est un homme intègre et droit, craignant Dieu et évitant le mal."
9 Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
Le Satan répliqua au Seigneur et dit: "Est-ce donc gratuitement que Job craint Dieu?
10 “Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
N’As-tu pas élevé comme une haie tutélaire autour de lui, de sa maison et de tout ce qui lui appartient? Tu as béni l’œuvre de ses mains, et ses troupeaux se répandent dans le pays.
11 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
Or ça, étends une fois ta main et touche tout ce qui est à lui; tu verras s’il ne te reniera pas en face."
12 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
L’Eternel répondit au Satan: "Eh bien! Tout ce qui lui appartient est en ton pouvoir; seulement, tu ne le toucheras pas lui-même." Et le Satan se retira de devant la face de l’Eternel.
13 Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
Un jour donc que les fils et les filles de Job mangeaient et buvaient du vin dans la maison de leur frère aîné,
14 wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
un messager aborda Job et lui dit: "Les bœufs étaient en train de labourer et les ânesses paissaient à: côté d’eux,
15 tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
quand les Sabéens ont fait irruption et les ont enlevés; quant aux esclaves, ils les ont passés au fil de l’épée; moi seul j’ai pu m’échapper et te l’annoncer."
16 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Il n’avait pas achevé de parler qu’un autre survient et dit: "Un feu de Dieu est tombé du ciel, embrasant les brebis et les esclaves, et a tout consumé. Moi seul j’ai pu m’échapper et te l’annoncer."
17 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
Il parlait encore qu’un autre arrive et dit: "Des Chaldéens, ayant formé trois bandes, se sont jetés sur les chameaux et les ont enlevés; quant aux esclaves, ils les ont passés au fil de l’épée. Moi seul j’ai pu m’échapper et te l’annoncer."
18 Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
Il n’avait pas fini de parler qu’un autre survient et dit: "Tes fils et tes filles mangeaient et buvaient dans la maison de leur frère aîné,
19 mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
et voilà qu’un vent violent, venant de l’autre côté du désert, a ébranlé les quatre angles de la maison; elle s’est écroulée sur les jeunes gens, et ils ont péri. Moi seul, j’ai pu m’échapper et te l’annoncer."
20 Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
Job se leva, déchira sa tunique, se rasa la tête, se jeta à terre et resta prosterné.
21 nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
Il dit: "Nu je suis sorti du sein de ma mère, et nu j’y rentrerai. L’Eternel avait donné, l’Eternel a repris, que le nom de l’Eternel soit béni!"
22 Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”
En dépit de tout, Job ne faillit point et n’imputa pas d’injustice à Dieu.

< Yobu 1 >