< Masalimo 35 >

1 Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
David’s. Contend, O Yahweh, with them who contend with me, Make war upon them who make war upon me.
2 Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
Grasp buckler and shield, and arise in my help;
3 Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
Then draw the spear, and close up against my pursuers, Say to my soul, Thy salvation, I am!
4 Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
Let them be ashamed and confounded, who are seeking my life, —Let them turn back and be put to the blush, who are devising my hurt:
5 Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
Let them be as chaff before the wind, with, the messenger of Yahweh, pressing them on:
6 Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
Let their way become dark and slippery, with, the messenger of Yahweh, pursuing them.
7 Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
For, without cause, have they hid for me, in a ditch, their net, —Without cause, have they digged [a pit] for my life.
8 chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
There shall reach him a ruin he could not know, —Yea, his own net which he hath hidden, shall capture him, Into that ruin, shall he fall!
9 Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
But, my soul, shall exult in Yahweh, —shall be glad in his salvation.
10 Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
All my bones, shall say—O Yahweh, who is like unto thee? Rescuing the oppressed from one stronger than he, Yea the oppressed and the needy, from their spoiler.
11 Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
There rise up witnesses helping forward violence and wrong, What I know not, they demand of me:
12 Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
They repay me evil for good, Bereaving my soul.
13 Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
But, as for me, when they were sick, my clothing was sackcloth, I humbled, with fasting, my soul, though, my prayer, unto mine own bosom, might return:
14 ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
Like as for a friend, like as for a brother of mine own, I walked to and fro, As though mourning for a mother, I gloomily bowed myself down.
15 Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
But, in mine overthrow, have they rejoiced, and gathered themselves together, —There gathered themselves together against me foolish men, and I knew it not, They have torn in pieces, and not been silent;
16 Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
Amidst profane praters of perversion, have they gnashed upon me with their teeth.
17 Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
My Lord! how long wilt thou look on? Bring back my soul out of their raging, from among lions, my solitary self.
18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
I will thank thee, in the midst of a great convocation, —In the midst of a mighty people, will I praise thee.
19 Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
Let not them who are falsely my foes rejoice over me, As for them who hate me without cause, let them not wink the eye!
20 Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
For, no salvation, will they utter, —But, against the quiet of the land, deceitful things, do they devise;
21 Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
Yea they have opened wide against me their mouth, They have said, Aha! Aha! our own eye, hath seen!
22 Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
Thou hast seen, O Yahweh, do not keep silence! O My Lord! be not far from me:
23 Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
Bestir thyself and wake up, to my vindication, O my God and My Lord!—to my plea:
24 Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
Vindicate me according to thy righteousness, O Yahweh, my God! And let them not rejoice over me:
25 Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
Let them not say in their heart, Aha! to our mind! Let them not say, We have swallowed him up!
26 Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
Let them turn pale, and then at once blush, who are rejoicing at my misfortune, —Let them be clothed with shame and confusion, who are magnifying themselves against me.
27 Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
Let them shout in triumph and rejoice, who are desiring my justification; And let them say continually, Yahweh be magnified, Who hath taken pleasure in the prosperity of his servant.
28 Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.
Mine own tongue also, shall softly utter thy righteousness, —All the day long, —thy praise!

< Masalimo 35 >