< Masalimo 34 >

1 Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
“By David, when he disguised his reason before Abimelech, who drove him away, and he departed.” I will bless the Lord at all times: continually shall his praise be in my mouth.
2 Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
My soul shall make her boast in the Lord: the humble shall hear it, and be rejoiced.
3 Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
Oh magnify the Lord with me, and let us exalt his name together.
4 Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
I sought the Lord, and he answered me, and from all that I dreaded did he deliver me.
5 Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
They [who] looked unto him, were indeed enlightened, and their faces were not put to the blush.
6 Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
This poor man cried, and the Lord heard him, and out of all his distresses did he save him.
7 Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
The angel of the Lord encampeth round about those who fear him, and delivereth them.
8 Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
Experience and see that the Lord is good: happy is the man that trusteth in him.
9 Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
Oh fear the Lord, ye his saints: for there is no want to those who fear him.
10 Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
The young lions do lack, and suffer hunger; but those who seek the Lord shall not want any good.
11 Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
Come, ye children, hearken unto me: the fear of the Lord will I teach you.
12 Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
Who is the man that desireth life, loveth [many] days, that he may see happiness?
13 asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
Guard thy tongue from evil, and thy lips from speaking deceit.
14 Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Depart from evil, and do good; seek peace, and pursue it.
15 Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
The eyes of the Lord are directed unto the righteous, and his ears unto their cry.
16 nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
[But] the anger of the Lord is against those that do evil, to cut off from the earth their remembrance.
17 Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
Those cry, and the Lord heareth, and from all their distresses he delivereth them.
18 Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
The Lord is nigh unto those that are broken-hearted: and he saveth those that are of a contrite spirit.
19 Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
Many are the afflictions of the righteous; but out of them all the Lord ever delivereth him.
20 Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
He watcheth all his bones: not one of them is broken.
21 Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
The evil will slay the wicked: and they who hate the righteous shall incur guiltiness.
22 Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
The Lord redeemeth the soul of his servants: and all that trust in him shall not incur guiltiness.

< Masalimo 34 >