< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Be joyful, O ye righteous, in the Lord; [for] unto the righteous praise is comely.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Give thanks unto the Lord with the harp: with the ten-stringed psaltery do ye sing [praises] unto him.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Sing unto him a new song; play beautifully amidst a triumphant shout.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
For the word of the Lord is upright; and all his works [are done] in truth.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
He loveth righteousness and justice: the earth is full of the kindness of the Lord.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
By the word of the Lord were the heavens made; and by the breath of his mouth all their host.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
He gathereth together like heaps the waters of the sea: he layeth up in store-houses the depths [of the sea].
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Let all the earth fear the Lord: of him stand in awe all the inhabitants of the world.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
For he spoke, and it came into being: he commanded, and it stood fast.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
The Lord frustrateth the resolves of the nations: he bringeth to nought the thoughts of the people.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
The counsel of the Lord will stand for ever, the thoughts of his heart from generation to generation.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Happy is the nation whose God is the Lord, the people whom he hath chosen for himself as a heritage.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
The Lord looketh from heaven; he seeth all the sons of men.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
From the place of his habitation he directeth his view upon all the inhabitants of the earth;
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
He fashioneth their hearts altogether; he hath regard to all their works.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
The king is not saved by the multitude of an army: a mighty man is not delivered by much strength.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Vain is the horse for victory: nor shall he deliver any by the greatness of his strength.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Behold, the eye of the Lord is upon those that fear him, upon those that hope for his kindness.
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
To deliver from death their soul, and to keep them alive in famine.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Our soul waiteth for the Lord: our help and our shield is he.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
For in him shall our heart rejoice: because in his holy name have we trusted.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Let thy kindness, O Lord, be upon us, even as we hope in thee.

< Masalimo 33 >