< Masalimo 27 >
1 Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
Psaume de David, avant qu’il fût oint.
2 Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
Tandis que des malfaiteurs s’apprêtent à fondre sur moi, pour manger mes chairs, Mes ennemis qui me tourmentent, ont été eux-mêmes affaiblis, et sont tombés.
3 Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
Si des camps s’établissent contre moi, mon cœur ne craindra pas. Si un combat est livré contre moi, j’y mettrai mon espérance.
4 Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
J’ai demandé une seule chose au Seigneur, je la rechercherai; c’est d’habiter dans la maison du Seigneur tous les jours de ma vie, C’est de contempler les délices du Seigneur et de visiter son temple.
5 Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
Car il m’a caché dans son tabernacle; au jour des malheurs il m’a protégé en me cachant dans son tabernacle.
6 Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
Il m’a élevé sur un rocher; et maintenant il a élevé ma tête au-dessus de mes ennemis.
7 Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Exaucez, Seigneur, ma voix par laquelle j’ai crié vers vous: ayez pitié de moi, et exaucez-moi.
8 Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
Mon cœur vous a parlé, ma face vous a recherché: je rechercherai, Seigneur, votre face.
9 Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
Ne détournez pas votre face de moi; ne vous retirez point, dans votre colère, de votre serviteur. Soyez mon aide; ne m’abandonnez pas, ne me méprisez pas, ô Dieu, mon Sauveur.
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
Parce que mon père et ma mère m’ont abandonné; mais le Seigneur m’a recueilli.
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
Prescrivez-moi, Seigneur, une loi à suivre dans votre voie; et conduisez-moi dans une voie droite à cause de mes ennemis.
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
Ne me livrez pas aux âmes de ceux qui m’affligent; parce que se sont élevés contre moi des témoins iniques, et que l’iniquité a menti contre elle-même.
13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Je crois que je verrai les biens du Seigneur dans la terre des vivants.
14 Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.
Attends le Seigneur, agis avec courage; et que ton cœur se fortifie, et attends avec constance le Seigneur.