< Masalimo 26 >

1 Salimo la Davide. Weruzeni Inu Yehova pakuti ndakhala moyo wosalakwa. Ndadalira Yehova popanda kugwedezeka.
Pour la fin, psaume de David.
2 Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni, santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
Éprouvez-moi, Seigneur, et sondez-moi; brûlez mes reins et mon cœur.
3 pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse, ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
Parce que votre miséricorde est devant mes yeux; et je me suis complu dans votre vérité.
4 Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo, kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
Je n’ai pas siégé dans un conseil de vanité; et je ne m’ingérerai pas parmi ceux qui commettent des iniquités.
5 Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
Je hais l’assemblée des méchants; et je ne siégerai pas avec des impies.
6 Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
Je laverai mes mains parmi des innocents, et je me tiendrai autour de votre autel, ô Seigneur;
7 kulengeza mofuwula za matamando anu ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
Afin que j’entende la voix de votre louange, et que je raconte toutes vos merveilles.
8 Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo, malo amene ulemerero wanu umapezekako.
Seigneur, j’ai aimé la beauté de votre maison, et le lieu où habite votre gloire.
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa, moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
Ne perdez pas, ô Dieu, mon âme avec des impies, ni ma vie avec des hommes de sang;
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa, dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
Dans les mains desquels sont des iniquités, dont la droite est remplie de présents.
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa; mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
Mais moi, j’ai marché dans mon innocence; rachetez-moi et ayez pitié de moi.
12 Ndayima pa malo wopanda zovuta ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
Mon pied est demeuré ferme dans la droite voie: dans les assemblées, je vous bénirai, Seigneur.

< Masalimo 26 >