< Masalimo 22 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
برای سالار مغنیان بر غزاله صبح. مزمور داود ای خدای من، ای خدای من، چرا مراترک کرده‌ای و از نجات من و سخنان فریادم دور هستی؟۱
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
‌ای خدای من در روز می خوانم و مرا اجابت نمی کنی. در شب نیز و مراخاموشی نیست.۲
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
و اما تو قدوس هستی، ای که بر تسبیحات اسرائیل نشسته‌ای.۳
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
پدران ما بر توتوکل داشتند. بر تو توکل داشتند و ایشان راخلاصی دادی.۴
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
نزد تو فریاد برآوردند و رهایی یافتند. بر تو توکل داشتند، پس خجل نشدند.۵
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
و اما من کرم هستم و انسان نی. عار آدمیان هستم و حقیر شمرده شده قوم.۶
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
هرکه مرا بیند به من استهزا می‌کند. لبهای خود را باز می‌کنند وسرهای خود را می‌جنبانند (و می‌گویند):۷
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
«برخداوند توکل کن پس او را خلاصی بدهد. او رابرهاند چونکه به وی رغبت می‌دارد.»۸
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
زیرا که تومرا از شکم بیرون آوردی؛ وقتی که بر آغوش مادر خود بودم مرا مطمئن ساختی.۹
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
از رحم برتو انداخته شدم. از شکم مادرم خدای من توهستی.۱۰
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
از من دور مباش زیرا تنگی نزدیک است. و کسی نیست که مدد کند.۱۱
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
گاوان نربسیار دور مرا گرفته‌اند. زورمندان باشان مرااحاطه کرده‌اند.۱۲
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
دهان خود را بر من باز کردند، مثل شیر درنده غران.۱۳
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
مثل آب ریخته شده‌ام. وهمه استخوانهایم از هم گسیخته. دلم مثل موم گردیده، در میان احشایم گداخته شده است.۱۴
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
قوت من مثل سفال خشک شده و زبانم به کامم چسبیده. و مرا به خاک موت نهاده‌ای.۱۵
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
زیراسگان دور مرا گرفته‌اند. جماعت اشرار مرا احاطه کرده، دستها و پایهای مرا سفته‌اند.۱۶
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
همه استخوانهای خود را می‌شمارم. ایشان به من چشم دوخته، می‌نگرند.۱۷
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
رخت مرا در میان خود تقسیم کردند. و بر لباس من قرعه انداختند.۱۸
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
اما تو‌ای خداوند دور مباش. ای قوت من برای نصرت من شتاب کن.۱۹
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
جان مرا از شمشیرخلاص کن. و یگانه مرا از دست سگان.۲۰
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
مرا ازدهان شیر خلاصی ده. ای که از میان شاخهای گاووحشی مرا اجابت کرده‌ای.۲۱
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
نام تو را به برادران خود اعلام خواهم کرد. در میان جماعت تو راتسبیح خواهم خواند.۲۲
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
‌ای ترسندگان خداوند او را حمد گویید. تمام ذریت یعقوب او را تمجید نمایید. و جمیع ذریت اسرائیل از وی بترسید.۲۳
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
زیرا مسکنت مسکین را حقیر و خوار نشمرده، و روی خود رااز او نپوشانیده است. و چون نزد وی فریاد برآورداو را اجابت فرمود.۲۴
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
تسبیح من در جماعت بزرگ از تو است. نذرهای خود را به حضورترسندگانت ادا خواهم نمود.۲۵
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
حلیمان غذاخورده، سیر خواهند شد. و طالبان خداوند او راتسبیح خواهند خواند. و دلهای شما زیست خواهد کرد تا ابدالاباد.۲۶
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
جمیع کرانه های زمین متذکر شده، بسوی خداوند بازگشت خواهندنمود. و همه قبایل امت‌ها به حضور تو سجده خواهند کرد.۲۷
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
زیرا سلطنت از آن خداونداست. و او بر امت‌ها مسلط است.۲۸
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
همه متمولان زمین غذا خورده، سجده خواهند کرد. وبه حضور وی هر‌که به خاک فرو می‌رود رکوع خواهد نمود. و کسی جان خود را زنده نخواهدساخت.۲۹
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
ذریتی او را عبادت خواهند کرد ودرباره خداوند طبقه بعد را اخبار خواهند نمود.۳۰
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
ایشان خواهند آمد و از عدالت او خبرخواهند داد، قومی را که متولد خواهند شد که اواین کار کرده است.۳۱

< Masalimo 22 >