< Masalimo 20 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
For the Leader. A Psalm of David. The LORD answer thee in the day of trouble; the name of the God of Jacob set thee up on high;
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Send forth thy help from the sanctuary, and support thee out of Zion;
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
Receive the memorial of all thy meal-offerings, and accept the fat of thy burnt-sacrifice; (Selah)
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Grant thee according to thine own heart, and fulfil all thy counsel.
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
We will shout for joy in thy victory, and in the name of our God we will set up our standards; the LORD fulfil all thy petitions.
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Now know I that the LORD saveth His anointed; He will answer him from His holy heaven with the mighty acts of His saving right hand.
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Some trust in chariots, and some in horses; but we will make mention of the name of the LORD our God.
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
They are bowed down and fallen; but we are risen, and stand upright.
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
Save, LORD; let the King answer us in the day that we call.