< Masalimo 147 >

1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
alleluia Aggei et Zacchariae laudate Dominum quoniam bonum psalmus Deo nostro sit iucunda decoraque; laudatio
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
aedificans Hierusalem Dominus dispersiones Israhel congregabit
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
qui sanat contritos corde et alligat contritiones illorum
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
qui numerat multitudinem stellarum et omnibus eis nomina vocans
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
magnus Dominus noster et magna virtus eius et sapientiae eius non est numerus
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
suscipiens mansuetos Dominus humilians autem peccatores usque ad terram
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
praecinite Domino in confessione psallite Deo nostro in cithara
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
qui operit caelum nubibus et parat terrae pluviam qui producit in montibus faenum et herbam servituti hominum
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
et dat iumentis escam ipsorum et pullis corvorum invocantibus eum
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
non in fortitudine equi voluntatem habebit nec in tibiis viri beneplacitum erit ei
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
beneplacitum est Domino super timentes eum et in eis qui sperant super misericordia eius
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
alleluia lauda Hierusalem Dominum lauda Deum tuum Sion
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
quoniam confortavit seras portarum tuarum benedixit filiis tuis in te
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
qui posuit fines tuos pacem et adipe frumenti satiat te
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
qui emittit eloquium suum terrae velociter currit sermo eius
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
qui dat nivem sicut lanam nebulam sicut cinerem spargit
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
mittit cristallum suum sicut buccellas ante faciem frigoris eius quis sustinebit
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
emittet verbum suum et liquefaciet ea flabit spiritus eius et fluent aquae
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
qui adnuntiat verbum suum Iacob iustitias et iudicia sua Israhel
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
non fecit taliter omni nationi et iudicia sua non manifestavit eis

< Masalimo 147 >