< Masalimo 146 >

1 Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Alleluia, Aggaei, et Zachariae.
2 Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
Lauda anima mea Dominum, laudabo Dominum in vita mea: psallam Deo meo quamdiu fuero. Nolite confidere in principibus:
3 Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
in filiis hominum, in quibus non est salus.
4 Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
Exibit spiritus eius, et revertetur in terram suam: in illa die peribunt omnes cogitationes eorum.
5 Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
Beatus, cuius Deus Iacob adiutor eius, spes eius in Domino Deo ipsius:
6 Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
qui fecit caelum et terram, mare, et omnia, quae in eis sunt.
7 Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
Qui custodit veritatem in saeculum, facit iudicium iniuriam patientibus: dat escam esurientibus. Dominus solvit compeditos:
8 Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
Dominus illuminat caecos. Dominus erigit elisos, Dominus diligit iustos.
9 Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
Dominus custodit advenas, pupillum et viduam suscipiet: et vias peccatorum disperdet.
10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.
Regnabit Dominus in saecula Deus tuus Sion, in generatione et generationem.

< Masalimo 146 >