< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Laudatio David. Exaltabo te Deus meus rex: et benedicam nomini tuo in saeculum, et in saeculum saeculi.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Per singulos dies benedicam tibi: et laudabo nomen tuum in saeculum, et in saeculum saeculi.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Magnus Dominus et laudabilis nimis: et magnitudinis eius non est finis.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Generatio et generatio laudabit opera tua: et potentiam tuam pronunciabunt.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Magnificentiam gloriae sanctitatis tuae loquentur: et mirabilia tua narrabunt.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Et virtutem terribilium tuorum dicent: et magnitudinem tuam narrabunt.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Memoriam abundantiae suavitatis tuae eructabunt: et iustitia tua exultabunt.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Miserator et misericors Dominus: patiens, et multum misericors.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Suavis Dominus universis: et miserationes eius super omnia opera eius.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Confiteantur tibi Domine omnia opera tua: et sancti tui benedicant tibi.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
Gloriam regni tui dicent: et potentiam tuam loquentur:
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
Ut notam faciant filiis hominum potentiam tuam: et gloriam magnificentiae regni tui.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Regnum tuum regnum omnium saeculorum: et dominatio tua in omni generatione et generationem. Fidelis Dominus in omnibus verbis suis: et sanctus in omnibus operibus suis.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Allevat Dominus omnes, qui corruunt: et erigit omnes elisos.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Oculi omnium in te sperant Domine: et tu das escam illorum in tempore opportuno.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Aperis tu manum tuam: et imples omne animal benedictione.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Iustus Dominus in omnibus viis suis: et sanctus in omnibus operibus suis.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Prope est Dominus omnibus invocantibus eum: omnibus invocantibus eum in veritate.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Voluntatem timentium se faciet, et deprecationem eorum exaudiet: et salvos faciet eos.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Custodit Dominus omnes diligentes se: et omnes peccatores disperdet.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Laudationem Domini loquetur os meum: et benedicat omnis caro nomini sancto eius in saeculum, et in saeculum saeculi.

< Masalimo 145 >